< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
The Spirit of the Lord is upon me, for the Lord has anointed me. He has sent me to bring good news to the meek, so as to heal the contrite of heart, to preach leniency to captives and release to the confined,
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
and so to proclaim the acceptable year of the Lord and the day of vindication of our God: to console all who are mourning,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
to take up the mourners of Zion and to give them a crown in place of ashes, an oil of joy in place of mourning, a cloak of praise in place of a spirit of grief. And there, they shall be called the strong ones of justice, the planting of the Lord, unto glorification.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
And they will rebuild the deserted places of past ages, and they will raise up the ruins of antiquity, and they will repair the desolate cities, which had been dissipated for generation after generation.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
And foreigners will stand up and will pasture your flocks. And the sons of sojourners will be your farmers and the workers of your vineyards.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
But you yourselves will be called the priests of the Lord. It will be said to you, “You are the ministers of our God.” You will eat from the strength of the Gentiles, and you will pride yourself on their glory.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Instead of your double confusion and shame, they will praise their portion. Because of this, they will possess double in their land. Everlasting joy will be for them.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
For I am the Lord, who loves judgment and who holds hatred for robbery within a burnt offering. And I will turn their work into truth, and I will forge a perpetual covenant with them.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
And they will know their offspring among the nations, and their progeny in the midst of the peoples. All who see them will recognize them: that these are the offspring whom the Lord has blessed.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
I will rejoice greatly in the Lord, and my soul will exult in my God. For he has clothed me with the vestments of salvation, and he has wrapped me in the clothing of justice, like a groom arrayed with a crown, and like a bride adorned with her jewels.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
For as the earth brings forth its seedlings and the garden produces its seeds, so will the Lord God bring forth justice and praise in the sight of all the nations.

< Yesaya 61 >