< Yesaya 39 >
1 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
Ob tistem času je babilonski kralj Merodáh Baladán poslal Ezekíju pisma in darilo, kajti slišal je, da je bil bolan in je okreval.
2 Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
Ezekíja jih je bil vesel in jim razkazal hišo svojih dragocenih stvari: srebro, zlato, dišave, dragoceno mazilo in vso hišo svoje orožarne in vsega, kar se je našlo v njegovih zakladnicah. Ničesar ni bilo v njegovi hiši niti v vsem njegovem gospostvu, česar jim Ezekíja ni razkazal.
3 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Potem je prerok Izaija prišel h kralju Ezekíju in mu rekel: »Kaj so rekli ti možje? In od kod so prišli k tebi?« Ezekíja je rekel: »K meni so prišli iz daljne dežele, celó iz Babilona.«
4 Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
Potem je rekel: »Kaj so videli v tvoji hiši?« Ezekíja je odgovoril: »Videli so vse, kar je v moji hiši. Ničesar ni med mojimi zakladi, česar jim ne bi pokazal.«
5 Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
Potem Izaija reče Ezekíju: »Poslušaj besedo Gospoda nad bojevniki:
6 Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
›Glej, prihajajo dnevi, da bo vse, kar je v tvoji hiši in to, kar so tvoji očetje prihranili v shrambi do tega dne, odneseno v Babilon. Nič ne bo ostalo, ‹ govori Gospod.
7 Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
›In izmed tvojih sinov, ki bodo izšli iz tebe, ki jih boš zaplodil, jih bodo odvedli proč in bodo evnuhi v palači babilonskega kralja.‹«
8 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”
Potem je Ezekíja rekel Izaiju: »Dobra je Gospodova beseda, ki si jo povedal.« Poleg tega je rekel: »Kajti mir in resnica bosta v mojih dneh.«