< Yesaya 37 >

1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
И бысть егда услыша царь Езекиа, растерза ризы и облечеся во вретище и вниде во храм Господень:
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
и посла Елиакима домостроителя, и Сомну книгочия, и старейшины жречески оболчены во вретища ко Исаии пророку сыну Амосову.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
И рекоша ему: сия глаголет Езекиа: день печали и укоризны и обличения и гнева днешний день, понеже прииде болезнь раждающей, крепости же не имеет родити:
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
да услышит Господь Бог твой словеса Рапсакова, яже посла царь Ассирийский, господин его, укаряти Бога живаго и поносити словесы, яже слыша Господь Бог твой, и да помолишися ко Господеви Богу твоему о оставшихся сих.
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
И приидоша отроцы царя Езекии ко Исаии.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
И рече им Исаиа: сице рцыте ко господину вашему: сия глаголет Господь: не убойся от словес, яже еси слышал, имиже укориша Мя послы царя Ассирийска:
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
се, Аз вложу в него дух, и услышав весть возвратится во страну свою и падет мечем на своей земли.
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
И возвратися Рапсак и обрете царя Ассирийскаго облежаща Ловну: и услыша царь Ассирийск, яко отиде от Лахиса,
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
и изыде Фарака царь Ефиопский воевати нань: и услышав возвратися и посла послы ко Езекии, глаголя:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
сице рцыте Езекии царю Иудейску: да не прельщает Бог твой тебе, на Негоже уповая еси, глаголя, яко не предастся Иерусалим в руце царя Ассирийска:
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
или не слышал еси ты, что сотвориша царие Ассирийстии, како всю землю погубиша, и ты ли избавишися?
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
Еда избавиша сих бози язычестии, ихже погубиша отцы мои Гозан и Харран и Расем, иже суть во стране Феемафи?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Где суть царие Емафовы, и где Арфафовы, и где града Епфаруема, Анагугана?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
И взя Езекиа книгу от послов и прочте ю, и вниде во храм Господень и отверзе ю пред Господем.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
И помолися Езекиа ко Господеви, глаголя:
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Господи Саваоф, Боже Израилев, седяй на Херувимех, Ты еси Бог един Царь всякаго царства вселенныя, Ты сотворил еси небо и землю:
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
приклони, Господи, ухо Твое, услыши, Господи, отверзи, Господи, очи Твои, призри, Господи, и виждь и слыши вся словеса Сеннахиримля, яже посла укаряти Бога живаго:
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
поистинне бо, Господи, пусту сотвориша царие Ассирийстии всю землю и страны их,
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
и ввергоша кумиры их во огнь, не беша бо бози, но дела рук человеческих, древа и камение, и погубиша я:
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
ныне же, Господи Боже наш, спаси ны от руки их, да уведят вся царствия земная, яко Ты еси (Господь) Бог един.
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
И послан бысть Исаиа сын Амосов ко Езекии и рече ему: сия глаголет Господь Бог Израилев: слышах, о нихже молился еси ко Мне о Сеннахириме цари Ассирийстем.
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
Сие слово, еже глагола о нем Бог: похули тя и поругася тебе девица дщи Сионя, на тя главою покива дщи Иерусалимля:
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
кого укорил и разгневал еси? Или к кому возвысил еси глас твой, и не воздвигл еси на высоту очес твоих? Ко Святому Израилеву!
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
Яко послами укорил еси Господа, ты бо рекл еси: множеством колесниц аз взыдох на высоту гор и на последняя Ливана, и посекох высоту кедра его и доброту кипарисову, и внидох в высоту части дубравныя
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
и положих мост, и опустоших воды и все собрание водное:
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
не слышал ли еси издревле сих, яже Аз сотворих? От древних дний совещах, ныне же показах опустошити языки в твердынех и живущыя во твердых градех:
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
опустих руце, и изсхоша и быша аки сухо сено на кровех и аки троскот:
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
ныне же покой твой и исход твой и вход твой Аз вем,
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
ярость же твоя, еюже разгневался еси, и огорчение твое взыде ко Мне, и вложу брозду в ноздри твоя, и узду во уста твоя, и возвращу тя путем, имже еси пришел.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
Сие же тебе знамение: яждь сего лета, еже еси всеял, а во второе лето, еже от себе растет: а в третие насеявше пожнете и насадите винограды и снесте плоды их:
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
и будут оставшии во Иудеи, прорастят корение долу и сотворят в верх плод,
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
яко от Иерусалима будут оставшиися и спасшиися от горы Сиони: ревность Господа Саваофа сотворит сия.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
Сего ради тако глаголет Господь на царя Ассирийска: не внидет в сей град, ниже пустит нань стрелу, ниже возложит нань щита, ниже оградит окрест его ограждения:
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
но путем, имже прииде, темже возвратится, и во град сей не внидет. Сия глаголет Господь:
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
защищу град сей, еже спасти его Мене ради и ради Давида раба Моего.
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
И изыде Ангел Господень и изби от полка Ассирийска сто осмьдесят пять тысящ. И воставше заутра, обретоша вся телеса мертва.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
И отиде возвращься Сеннахирим царь Ассирийский и вселися во Ниневии.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
И внегда покланятися ему и в дому Насараху отечествоначалнику своему, Адрамелех и Сарасар сынове его убиста его мечьми, сами же убежаста во Армению. И воцарися Асордан сын его вместо его.

< Yesaya 37 >