< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Приступите, языцы, и услышите, князи: да слышит земля и живущии на ней, вселенная и людие, иже на ней.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
Зане ярость Господня на вся языки и гнев на число их, еже погубити их и предати я на заклание.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
И язвении их повергнутся и мертвецы, и взыдет их смрад, и намокнут горы кровию их:
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
и истают вся силы небесныя, и свиется небо аки свиток, и вся звезды спадут яко листвие с лозы, и якоже спадает листвие смоковницы.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Упися мечь Мой на небеси: се, на Идумею снидет и на люди пагубныя с судом.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Мечь Господень наполнися крове, растолсте туком, от крове козлов и агнцев и от тука козлов и овнов: яко жертва Господеви в Восоре, и заклание велие во Идумеи.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
И падут с ними сильнии, и овны и юнцы, и упиется земля от крове и от тука их насытится:
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
день бо суда Господня, и лето воздаяния суда Сионя.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
И обратятся дебри его в смолу, и земля его в жупел,
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
и будет земля его горящи яко смола днем и нощию, и не угаснет в вечное время, и взыдет дым ея высоце, в роды своя опустеет.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
И во время много птицы и ежеве, совы и вранове возгнездятся в нем: и возложат нань уже землемерно пустыни, и онокентаври вселятся в нем.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
Князи его не будут: царие бо и вельможи его будут в пагубу.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
И возникнут во градех их терновая древеса и во твердынех его, и будут селения сирином и селища струфионом:
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
и срящутся беси со онокентавры и возопиют друг ко другу, ту почиют онокентаври, обретше себе покоища:
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
тамо возгнездится ежь, и сохранит земля дети его со утверждением: тамо елени сретошася и увидеша лица друг друга.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Числом преидоша, и един и них не погибе, друг друга не взыска, яко Господь заповеда им, и дух Его собра я.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
И Той вержет им жребия, и рука Его раздели пастися: в вечное время наследите, в роды родов почиют в нем.

< Yesaya 34 >