< Yesaya 25 >
1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
PANIE, ty jesteś moim Bogiem; będę cię wywyższać i wysławiać twoje imię, bo uczyniłeś cudowne rzeczy; twoje postanowienia, z dawna powzięte, są wiernością i prawdą.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Bo obróciłeś miasto w rumowisko, miasto obronne w ruiny. Pałac cudzoziemców przestał być miastem, nigdy nie będzie odbudowany.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Dlatego będzie cię wielbić lud mocny; miasto okrutnych narodów będzie się ciebie bać.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Ty bowiem jesteś twierdzą dla ubogiego, twierdzą dla nędzarza w jego ucisku, ucieczką przed powodzią, zasłoną przed upałem, gdy wściekłość okrutników jest jak powódź bijąca w ścianę.
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
Wrzawę cudzoziemców stłumisz jak upał na wysuszonej ziemi, jak upał – cieniem obłoku. Okrucieństwo okrutników będzie poniżone.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Na tej górze PAN zastępów wyprawi wszystkim ludom ucztę z tłustych potraw, ucztę z wystałego wina, z tłustych potraw ze szpikiem, z wina wystałego i czystego.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
I zniszczy na tej górze zasłonę rozpostartą nad wszystkimi ludźmi i przykrycie rozciągnięte nad wszystkimi narodami.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
Połknie śmierć w zwycięstwie, a Pan BÓG otrze łzy z każdego oblicza i zdejmie z całej ziemi hańbę swego ludu, bo tak PAN powiedział.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
I w tym dniu będzie się mówić: Oto nasz Bóg, jego oczekiwaliśmy i on nas wybawi. To jest PAN, jego oczekiwaliśmy; będziemy się weselić i radować z jego zbawienia.
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Na tej górze bowiem spocznie ręka PANA, a Moab będzie zdeptany przez niego, jak depcze się słomę na gnojowisku.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
I rozciągnie swoje ręce pośrodku niego, jak je rozciąga pływak, by pływać, i poniży jego wyniosłość wraz z wysiłkami jego rąk.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
A twoje wysokie mury obronne obali, zburzy i zrzuci na ziemię – [obróci je] w proch.