< Yesaya 25 >

1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Nkosi unguNkulunkulu wami; ngizakuphakamisa, ngidumise ibizo lakho; ngoba wenzile okumangalisayo; amacebo akho endulo aluthembeko leqiniso.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Ngoba wenzile umuzi waba yinqwaba; umuzi obiyelweyo ube lunxiwa; isigodlo sabezizwe singabi ngumuzi; kasiyikwakhiwa kuze kube nininini.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Ngenxa yalokho abantu abalamandla bazakudumisa; umuzi wezizwe ezilesihluku uzakwesaba.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Ngoba ubungamandla kumyanga, amandla kosweleyo ekuhluphekeni kwakhe, isiphephelo kuzulu lesiphepho, umthunzi ekutshiseni, lapho ukuvuthela kwabalolunya kunjengezulu lesiphepho emdulini.
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
Uzakwehlisa umsindo wabezizwe njengokutshisa endaweni eyomileyo; ukutshisa emthunzini weyezi; ingoma yabalolunya izathotshiswa.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Lakulintaba iNkosi yamabandla izakwenzela abantu bonke idili lezinto ezinonileyo, idili lamawayini alenzece, lezinto ezinonileyo zigcwele umnkantsho, lamawayini alenzece acengekileyo.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
Izaginya kulintaba ubuso besembeso esembese bonke abantu, lesigubuzelo eselukiweyo phezu kwezizwe zonke.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
Izaginya ukufa ekunqobeni, leNkosi uJehova izakwesula inyembezi izisuse ebusweni bonke, isuse lehlazo labantu bayo emhlabeni wonke; ngoba iNkosi ikhulumile.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
Kuzakuthiwa-ke ngalolosuku: Khangela, lo nguNkulunkulu wethu; silindele kuye, njalo uzasisindisa; le yiNkosi; siyilindele, sizathaba, sithokoze kusindiso lwayo.
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Ngoba isandla seNkosi sizaphumula kulintaba, loMowabi uzanyathelelwa phansi kwayo, njengamahlanga abuthelelweyo enyathelelwa enqunjini yomquba.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
Njalo izakwelula izandla zayo phakathi kwakhe njengontshezayo ezelula ukuze antsheze; njalo izathobisa ukuzigqaja kwakhe kanye lokucathamela kwezandla zakhe.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
Lenqaba ephakemeyo yemiduli yakho izayidilizela phansi, iyehlisele phansi, iyifikise emhlabathini, ethulini.

< Yesaya 25 >