< Yesaya 25 >

1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Yahweh, you are my God; I will honor you and praise you [MTY]. You do wonderful things; you said long ago that you would do those things, and now you have done them like you said that you would.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
[Sometimes] you have caused cities to become heaps of rubble, cities that had strong walls around them. You have caused palaces in foreign countries to disappear; they will never be rebuilt.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Therefore, people in powerful nations will declare that you are very great, and people in nations [whose leaders are] ruthless/cruel will revere you.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Yahweh, you are [like] [SIM] a strong tower where poor people can (find refuge/be safe), a place where needy people can go when they are distressed. [You are like] [MET] a place where people can find refuge in a storm and where they can be shaded from the hot sun. Ruthless/Cruel [people] oppress us; they are like [SIM] a storm beating against a wall,
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
and like [SIM] [the intense] heat in the desert. [But] you cause the roaring of people in foreign nations to cease. Like the air cools when a cloud comes overhead, you stop ruthless/cruel [people] from singing songs boasting about their being very great.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Here in Jerusalem, the Commander of the armies of angels will prepare a wonderful feast for all the people [of the world]. It will be a banquet with plenty of good meat and fine well-aged [DOU] wine.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
[People here are] sad; their being sad is [like] a dark cloud that hangs over them, like they experience when someone dies. But Yahweh will enable them to quit being sad.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
He will get rid of death forever! Yahweh our God will cause people to no longer mourn because someone has died. And he will stop other people insulting and making fun of his land and [us] his people. [That will surely happen because] Yahweh has said it!
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
At that time, [people] will proclaim, “Yahweh is our God! We trusted in him, and he rescued us! Yahweh, in whom we trusted, has done it; we should rejoice because of his saving/rescuing [us]!”
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Yahweh [MTY] will protect and bless Jerusalem. [But] he will crush [the people in the land of] Moab; they will be like [SIM] straw that is trampled in the manure [and left to rot].
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
Yahweh will push down the people of Moab like [SIM] a swimmer pushes [the water] with his hands. He will cause them to cease being proud, and he will show that all the things that they have done are worthless.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
The high walls [around the cities] in Moab will be torn down; they will be demolished and fall into the dust/dirt.

< Yesaya 25 >