< Yesaya 25 >
1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
O Jehovah, thou art my God; I will exalt thee; I will praise thy name, For thou hast done wonderful things; Thine ancient purposes are faithfulness and truth.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Thou hast made the city a heap; The fortified city a ruin. The palace of the barbarians is to be no more a city! It shall never be built again.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Therefore shall mighty kingdoms praise thee; The cities of the terrible nations shall honor thee;
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
For thou hast been a defence to the poor; A defence to the needy in his distress; A refuge from the storm, a shadow from the heat, When the rage of tyrants was like a storm against a wall.
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
As heat in a dry land is made to vanish, So thou puttest down the tumult of the barbarians; As heat is allayed by a thick cloud, So the triumph of the tyrants is brought low.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Then in this mountain shall Jehovah of hosts prepare for all nations A feast of fat things, and wines kept on the lees; Of fat things full of marrow, of wines kept on the lees well refined.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
He will destroy in this mountain the covering that was cast over all people, And the veil that was spread over all nations.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
He will destroy death forever; The Lord Jehovah will wipe away the tears from all faces, And the reproach of his people will he take away from the whole earth; For Jehovah hath said it.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
In that day shall men say, “Behold, this is our God; We waited for him, and he hath saved us; This is Jehovah, for whom we waited; Let us rejoice and exult in his salvation.”
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
For the hand of Jehovah shall rest upon this mountain, And Moab shall be trodden down in his place, As straw is trodden down in a dung-pool.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
And he shall stretch out his hands in the midst of it, As the swimmer stretcheth out his hands to swim, But God shall put down his pride, Together with the devices of his hands.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
And the high bulwarks of thy walls will he lay low; He will bring them down to the ground; he will lay them in the dust.