< Yesaya 25 >

1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Yaye Jehova Nyasaye, in Nyasacha; abiro miyi duongʼ kendo anapak nyingi, nimar kuom adiera mowinjore isetimo gik makare, mago mane osechan chon.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Isemiyo dala maduongʼ omukore, modhurore pidhe pidhe, dalano mochiel motegno okethore, dala maduongʼ ma jopinje mamoko noketoe genogi oserumo; bende ok nochak ogere kendo.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Kuom mano joma roteke nomiyi duongʼ; mier madongo mag ogendini ma jonjore biro miyi luor.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Isebedo kar pondo ne jochan, kar gengʼruok ne jodhier manie lit, kar bwok ka ahiti kudho, kendo kar tipo ka chiengʼ kech. Nimar muya mar janjore chalo mana ka ahiti makudho kochomo ohinga,
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
kendo mana ka liet manie piny motimo ongoro. Isetieko koko mar jopinje mamoko mana kaka tipo mar bor polo gengʼo liet, e kaka wend jonjore osechung.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Ewi godni Jehova Nyasaye Maratego biro loso nyasi mar chiemo mamiyo ne oganda duto, sawo mar divai mosekan, kod chiemo mabeyo gi divai molos maber.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
Ewi godni obiro walo law moumo wangʼ ji duto, law mogengʼo ogendini duto;
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
kendo enotiek tho chuth. Jehova Nyasaye Manyalo Gik Moko Duto biro yweyo pi wangʼ ji duto; mi nogol ajara kuom joge e piny duto. Jehova Nyasaye ema osewacho.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
E kindeno giniwach ni, “Adier ma en Nyasachwa; ne wageno kuome, kendo ne oresowa. Ma en Jehova Nyasaye, ne wageno kuome; wabeduru gi mor kendo gi ilo kuom warruokne.”
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Lwet Jehova Nyasaye biro yweyo ewi godni, to Moab nonyon piny gi tiende, mana kaka inyono lum e dipo.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
Giniyar badgi kuome, mana kaka ngʼama goyo abal yaro bedene ka kwangʼ. Nyasaye biro tieko sungagi kata obedo ni lwetgi riek e yor goyo abal.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
Obiro muko piny kuondeu mochiel motegno motingʼore gi malo mi oketgi piny, enotergi e lowo ma gilokre buru.

< Yesaya 25 >