< Yesaya 25 >
1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Herre! du er min Gud, jeg vil ophøje dig, jeg vil bekende dit Navn; thi du gjorde Under; de Raad, som ere fattede længe tilforn, ere Trofasthed og Sandhed.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Thi du gjorde af Staden en Stenhob, af den faste Stad en Grushob, de fremmedes Paladser ere ikke længer en Stad; den skal ikke bygges evindelig.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Derfor skal et mægtigt Folk ære dig; grumme Hedningers Stæder skulle frygte dig.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Thi du var den ringes Styrke, den fattiges Styrke, da han var i Angest, en Tilflugt imod Regnskyl, en Skygge imod Heden; thi de grummes Fnysen er som Regnskyl imod en Væg.
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
Som Heden i det tørre Land, saa nedtrykker du de fremmedes Bulder; som Heden ved Skyggen af en Sky, saa dæmpes de grummes Sang.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
Og den Herre Zebaoth skal gøre for alle Folkeslag et fedt Gæstebud paa dette Bjerg, et Gæstebud med gammel Vin, med fed Marv, med gammel, klaret Vin.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
Og paa dette Bjerg skal han borttage Sløret, med hvilket alle Folkeslag ere tilslørede, og Dækket, hvormed alle Hedninger ere bedækkede.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
Han skal opsluge Døden for evig, og den Herre, Herre skal afviske Graaden af alle Ansigter og borttage sit Folks Forsmædelse af al Jorden; thi Herren har talt det.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
Og man skal sige paa den Dag: Se, dette er vor Gud, vi have haabet paa ham, og han skal frelse os; dette er Herren, vi have haabet paa ham, vi ville fryde og glæde os ved hans Frelse.
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Thi Herrens Haand skal hvile over dette Bjerg; men Moab skal nedtrædes, som man nedtræder Halm i Møddingpølen.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
Og det skal brede sine Hænder ud deri, ligesom den, der svømmer, udbreder dem for at svømme; og han skal nedtrykke dets Hovmod tillige med dets Hænders Ranker.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
Og dine høje Mures Befæstning skal han styrte, nedkaste, slaa til Jorden indtil Støvet.