< Yesaya 25 >
1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Jahve, ti si Bog moj, uznosim te, tvoje ime slavim, jer si proveo čudesan naum, smišljen od davnine, istinit i vjeran,
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
jer grad si pretvorio u hrpu kamenja, a mjesto utvrđeno u ruševine. Tvrđa neprijateljska više nije grad, dovijeka se više obnoviti neće.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Zato te slavi narod snažan, grad moćnih plemena tebe se boji;
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
jer ti si utočište nevoljnom, utočište ubogom u nevolji; ti si skrovište od pljuska i od žege zaklon, jer ćud je silnička kao pljusak zimski;
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
kao žega nad zemljom sušnom ti gušiš graju neprijatelja; kao žega sjenom oblaka prekinu se silniku pjesma pobjednička.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
I Jahve nad Vojskama spremit će svim narodima na ovoj gori gozbu od pretiline, gozbu od izvrsna vina, od pretiline sočne, od vina staložena.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
Na ovoj gori on će raskinuti zastor što zastiraše sve narode, pokrivač koji sva plemena pokrivaše
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
i uništit će smrt zasvagda. I suzu će sa svakog lica Jahve, Gospod, otrti - sramotu će svog naroda na svoj zemlji skinuti: tako Jahve reče.
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
I reći će se u onaj dan: “Gle, ovo je Bog naš, u njega se uzdasmo, on nas je spasio; ovo je Jahve u koga se uzdasmo! Kličimo i veselimo se spasenju njegovu,
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
jer ruka Jahvina na ovoj gori počiva!” Moab je izgažen na svome mjestu kao što se gazi slama na buništu;
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
ondje on razmahuje rukama kao što ih razmahuje plivač kada pliva. Ali Jahve obara njegovu ponositost i propinjanja ruku njegovih.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
Visoku tvrđu tvojih zidina on razvaljuje, na zemlju baca, u prah ruši.