< Yesaya 25 >

1 Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
Господи, Ти си мой Бог; Ще Те превъзнасям, ще пея хваления на името Ти; Защото си извършил чудни дела, Отдавнашните Си намерения, с вярност и истинност.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
Защото Ти обърна град в грамада, Укрепен град на развалина. Палатът на чужденците да не е град; Той никога няма да се съгради.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
Затова силните люде ще Те славят, Градът на страшните народи ще се бои от Тебе.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
Защото си бил крепост на сиромаха, Крепост на бедния в утеснението му, Прибежище от буря, сянка от пек, Когато устремът на насилниците нападне като буря върху стена.
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
Ще намалиш шума на чужденците Както пека в сухо място; Както пека чрез сянката на облак, Възклицанието на страшните ще ослабне.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
И на тоя хълм Господ на Силите ще направи на всичките племена Угощение от тлъсти неща, угощение от вина дълго стояли на дрождията си, От тлъсти неща пълни с мозък, От вина, дълго стояли на дрождията си, пречистени.
7 Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
И на тоя хълм Той ще развали Вънкашното покривало, което е мятано върху всичките племена, И покривката, която е простряна върху всичките народи.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
Ще погълне смъртта за винаги; И Господ Бог ще обърше сълзите от всичките лица, И ще отнеме укора на людете Си от цялата земя; Защото Господ е изговорил това,
9 Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
И в оня ден ще рекат: Ето, Тоя е наш Бог; Чакахме Го, и Той ще ни спаси; Тоя е Господ; чакахме Го; Ще се зарадваме и развеселим в спасението Му.
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
Защото в тоя хълм Господната ръка ще почине; И Моав ще бъде потъпкан на мястото си, Както се тъпче плявата в бунището.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
Господ ще разпростре ръцете Си всред него, Както плаващият простира ръце да плава, И ще повали гордостта му Въпреки лукавщината на ръцете му.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.
Ще сниши и крепостта ти, силна с високи стени, Ще я събори и хвърли на земята, дори в пръстта.

< Yesaya 25 >