< Yesaya 18 >

1 Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
Voi sitä maata, joka vaeltaa siipein varjon alla, tällä puolella Etiopian virtoja!
2 Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
Joka sanansaattajat lähettää merelle, ja kulkee vedellä ruokoisessa haahdessa: menkäät nopiasti matkaan, sanansaattajat, sen kansan tykö, joka reväisty ja ryöstetty on, sen kansan tykö, joka julmempi on kuin joku muu, sen kansan tykö, joka siellä ja täällä mitattu ja tallattu on, jonka maa virtain hallussa on.
3 Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
Te kaikki, jotka asutte maan päällä, ja te, jotka maassa olette, saatte nähdä, kuinka lippu nostetaan vuorella, ja kuulla, kuinka vaskitorvella soitetaan.
4 Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
Sillä näin sanoo Herra minulle: minä olen hiljakseni ja katselen majastani, niinkuin palavuus, joka sateen kuivaa, ja niinkuin kaste elonajan palavuudessa.
5 Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
Sillä ennen elonaikaa, kuin tulo valmiiksi tulee, ja rohkamarjat kypsentyvät, täytyy oksat leikata sirpillä, ja viinapuut hakata ja heittää pois:
6 Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
Niin että ne jätetään kokonansa linnuille vuorten päällä ja eläimille maassa; niin että linnut suvella tekevät siihen pesänsä, ja kaikkinaiset eläimet makaavat siinä talvella.
7 Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.
Silloin se revitty ja ryöstetty kansa, joka julmempi on kuin joku muu, joka siellä ja täällä mitattu on ja tallattu on, jonka maa virtain hallussa on, tuo Herralle Zebaotille lahjoja siihen paikkaan, jossa Herran Zebaotin nimi on, Zionin vuorelle.

< Yesaya 18 >