< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Salomon korkea veisu.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Hän suuta antakoon minun, suunsa antamisella; sillä sinun rakkautesi on suloisempi kuin viina,
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Sinun hyväin voidettes hajuin tähden. Sinun nimes on vuodatettu öljy; sen piikaiset sinua rakastavat.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Vedä minua, niin me juoksemme perässäs: Kuningas vie minun kammioonsa: Me iloitsemme ja riemuitsemme sinusta, me muistamme sinun rakkauttas enempi kuin viinaa: hurskaat rakastavat sinua.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Minä olen musta, mutta sangen otollinen, te Jerusalemin tyttäret, niinkuin Kedarin majat, niinkuin Salomon kirjoiteltu vaate.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Älkäät sitä katsoko, että minä niin musta olen; sillä päivä on minun polttanut: minun äitini lapset vihastuivat minun päälleni: he ovat asettaneet minun viinamäen vartiaksi, mutta en minä varjellut viinamäkeäni.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Sano minulle sinä, jota minun sieluni rakastaa: kussas laidunta pidät, ja kussas lounaalla lepäät? ettei minun pitäisi poikkeeman kumppanies lauman tykö.
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Jos et sinä sinuas tunne, sinä kaikkein ihanaisin vaimoin seassa, niin mene lammasten jäljille, ja kaitse vohlias paimenien huonetten tykönä.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Minä vertaan sinun, ystäväni, ratsaskaluihini, Pharaon vaunuihin.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Sinun sasupääs ovat ihanat pankkuin keskellä, ja sinun kaulas kultakäädyissä.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Me teemme sinulle kultaiset pankut, hopianastoilla.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Kuin kuningas istui pöytänsä tykönä, antoi nardukseni hajunsa.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Ystäväni on minun mirrhamkimppuni, joka minun rinnoillani riippuu.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Minun ystäväni on minulle Kyprin viinamarjan rypäle, Engeddin viinamäessä.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Katso, armaani, sinä olet ihana: katso, sinä olet ihana, silmäs ovat niinkuin kyhkyläisen silmät.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Katso, ystäväni, sinä olet ihana ja suloinen, ja meidän vuoteemme myös viheriöitsee.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Meidän huoneemme kaaret ovat sedripuusta, vuolteet hongasta.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >