< Yesaya 16 >
1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Sela'dan çöl yoluyla Siyon Kenti'nin kurulduğu dağa, Ülkenin hükümdarına kuzular gönderin.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
Moavlı kızlar yuvalarından atılmış, Öteye beriye uçuşan kuşlar gibi Arnon Irmağı'nın geçitlerinde dolaşıyor.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
“Bize öğüt ver, bir karar al, Öğle sıcağında gece gibi gölge sal üstümüze. Kovulanları sakla, kaçakları ele verme” diyorlar.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
“Kovulanlarım seninle birlikte yaşasın. Kırıp geçirenlere karşı Biz Moavlılar'a sığınak ol.” Baskı ve yıkım son bulduğunda, Ülkeyi çiğneyenler yok olduğunda, Sevgiye dayanan bir yönetim kurulacak,
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Davut soyundan biri sadakatle krallık yapacak. Yargılarken adaleti arayacak, Doğru olanı yapmakta tez davranacak.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
Moav'ın ne denli gururlanıp büyüklendiğini, Kendini ne denli beğendiğini, Kibirlenip küstahlaştığını duyduk. Övünmesi boşunadır.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
Bu yüzden Moavlılar Moav için feryat edecek, Hepsi feryat edecek. Kîr-Hereset'in üzüm pestillerini Anımsayıp üzülecek, yas tutacaklar.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
Çünkü Heşbon'un tarlaları, Sivma'nın asmaları kurudu. Ulusların beyleri onların seçkin dallarını kırdılar. O dallar ki, Yazer'e erişir, çöle uzanırdı, Filizleri yayılır, gölü aşardı.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
Bu yüzden Yazer için, Sivma'nın asmaları için acı acı ağlıyorum. Sizleri gözyaşlarımla sulayacağım, Ey Heşbon ve Elale! Çünkü savaş çığlıkları yaz meyvelerinizin, Biçtiğiniz ekinin üzerine düştü.
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
Meyve bahçelerindeki sevinç ve neşe yok oldu. Bağlarda ne şarkı söyleyen olacak, Ne sevinç çığlığı atan. Üzüm sıkma çukurlarında çalışan kalmayacak, Sevinç çığlıklarını susturdum.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
Yüreğim bir lir gibi inliyor Moav için, Kîr-Hereset için içim sızlıyor.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
Moav halkı tapınma yerine çıkarak kendini yoruyor, Dua etmek için tapınağa gidiyor, ama hepsi boşuna!
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
RAB'bin Moav için geçmişte söylediği budur.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
RAB şimdi diyor ki, “Moav'ın övündükleri de kalabalık halkı da tam üç yıl sonra rezil olacak. Sağ kalan çok az sayıda kişiyse güçsüz olacak.”