< Yesaya 15 >
1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Moav'la ilgili bildiri: Moav'ın Ar Kenti bir gecede viraneye döndü, yok oldu, Moav'ın Kîr Kenti bir gecede viraneye döndü, yok oldu.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Bu yüzden Divon halkı ağlamak için tapınağa, Tapınma yerlerine çıktı. Moav halkı, Nevo ve Medeva için feryat ediyor. İnsanlar saçlarını sakallarını kesiyor.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Çul giyiyorlar sokaklarda, Damlarda, meydanlarda herkes feryat ediyor, Gözyaşları sel gibi.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
Heşbon ve Elale'nin haykırışları Yahas'a ulaşıyor. Moav askerleri bu yüzden feryat ediyor, Yürekleri korku içinde.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Yüreğim sızlıyor Moav için. Kaçanlar Soar'a, Eglat-Şelişiya'ya ulaştı, Ağlaya ağlaya çıkıyorlar Luhit Yokuşu'ndan, Horonayim yolunda yıkımlarına ağıt yakıyorlar.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Nimrim suları kuruduğu için otlar sararıp soldu. Taze ot kalmadı, yeşillik yok artık.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Bu yüzden halk kazanıp biriktirdiği ne varsa, Kavak Vadisi üzerinden taşıyacak.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Haykırışları Moav topraklarında yankılanıyor, Feryatları Eglayim'e, Beer-Elim'e dek ulaştı.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Çünkü Dimon suları kan dolu, Ama başına daha beterini getireceğim. Moav'dan kaçıp kurtulanların, Ülkede sağ kalanların üzerine aslan salacağım.