< Yesaya 16 >

1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Lähettäkäät maaherran karitsat Selasta korven tyköä Zionin tyttären vuorelle.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
Mutta niinkuin lintu lentää pois, joka pesästänsä ajettu on, niin pitää Moabin tyttärelle tapahtuman Arnonin luotuspaikoissa.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
Pitäkäät neuvoa yhdessä, sanokaat tuomio, tee sinulles puolipäivän varjo niinkuin yö; kätke pois ajetut, ja älä ilomoita kulkioita.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Anna minun pois ajettuni asua tykönäs; ole Moab heidän varjeluksensa hävittäjää vastaan; niin vaivaaja saa lopun, kukistaja lakkaa, ja sotkuja taukoo maassa.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Mutta istuin valmistetaan armosta yhdelle istua, totuudessa, Davidin majassa, tuomita ja etsiä oikeutta, ja pikaisesti toimittaa vanhurskautta.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
Mutta me kuulemme Moabin ylpeydestä, että hän on aivan ylpeä, niin että hänen ylpeytensä, koreutensa ja vihansa on suurempi kuin hänen voimansa.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
Sentähden pitää yhden Moabilaisen itkemän toista, heidän pitää kaikkein itkemän; KirHaresetin (kaupungin) perustuksia pitää teidän huokaaman: ne ovat peräti kukistetut.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
Sillä Hesbon on tullut autioksi maaksi, Sibmassa ovat viinapuut turmellut, pakanain herrat ovat sotkuneet hänen parhaat viinapuunsa, ja tulleet Jaeseriin asti, ja vaeltaneet korpea ympäri; hänen viina-oksansa ovat hajoitetut ja viedyt meren ylitse.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
Sentähden minä itken Jaeserin tähden, ja Sibman viinapuun, ja vuodatan monta pisaraa Hesbonin ja Elalen tähden; sillä huuto on langennut sinun suvees ja tuloos!
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
Niin että ilo ja riemu lakkaa kedolla, ja ei viinamäissä iloita eikä huudeta, eli puserreta viinaa kuurnissa; minä olen lopettanut ilohuudon.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
Sentähden minun sydämeni kumisee Moabin tähden kuin kantele, ja minun sisällykseni KirHareksen tähden.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
Silloin pitää ilmoitettaman, kuinka Moab on väsynyt korkeuksissa ja mennyt kirkkoonsa rukoilemaan, ja ei kuitenkaan ole mitään aikoin saanut.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
Tämä on se, minkä Herra siihen aikaan puhui Moabia vastaan.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
Mutta nyt puhuu Herra ja sanoo: kolmena vuonna, niinkuin palvelian vuodet ovat, pitää Moabin kunnian, joka suuri on kaikissa kansoissa, tuleman pieneksi, niin että aivan vähä pitää jäämän, ja ei paljo.

< Yesaya 16 >