< Yesaya 11 >

1 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
Dua foforo bi befifi wɔ Yisai dunsin ho; efi ne ntin mu na Dubaa bi bɛsow aba.
2 Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
Awurade Honhom bɛtena ne so, nyansa ne ntease Honhom, afotu ne tumi Honhom, nimdeɛ ne Awurade suro Honhom,
3 Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
Na nʼani begye wɔ Awurade suro mu. Ɛnyɛ nea ɔde nʼani hu so na obegyina abu atɛn, anaa nea ɔde nʼaso bɛte so na obegyina asi gyinae;
4 koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
na mmom ɔde trenee bebu mmɔborɔfo atɛn, ɔde atɛntrenee besi gyinae ama asase so ahiafo. Ɔde nʼano abaa na ɛbɛbɔ asase; ɔde nʼanofafa home bekunkum amumɔyɛfo.
5 Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
Trenee bɛyɛ nʼabɔso na nokwaredi ayɛ nʼabɔso.
6 Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
Pataku ne oguamma bɛtena, ɔsebɔ ne abirekyi bɛda, nantwi ba ne gyata ne ne ba bɛbɔ mu; na abofra ketewa bi adi wɔn anim.
7 Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
Nantwi ne sisi bɛbɔ mu adidi, wɔn mma bɛdeda faako, na gyata bɛwe wura te sɛ nantwi.
8 Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
Akokoaa bedi agoru abɛn ɔprammiri amoa ano, na abofra ketewa de ne nsa ahyɛ ahurutoa bon mu.
9 Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
Wɔrenyɛ obi bɔne na wɔrensɛe ade wɔ me bepɔw Kronkron nyinaa so, na Awurade ho nimdeɛ bɛyɛ asase so ma sɛnea nsu ayɛ po ma no.
10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
Na da no, Yisai aseni bɛsɔre; nea ɔbɛsɔre abedi aman aman no so; ɔno na wɔn ani bɛda ne so, na nʼahomegyebea benya anuonyam.
11 Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
Saa da no, Awurade bɛma ne nsa so ne mprenu so de agye ne nkurɔfo a wɔaka afi Asiria, Misraim anafo fam, Misraim atifi fam, Kus, Elam, Babilonia, Hamat ne Po so asupɔw.
12 Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
Ɔbɛma frankaa so ama aman no na wɔaboaboa Israelfo a wɔatwa wɔn asu no ano; Ɔbɛboaboa Yudafo a wɔahwete no ano afi asase ntwea anan no so.
13 Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
Efraim anibere betu ayera, na wɔbɛsɛe Yuda atamfo. Efraim ani remmere Yuda bio, na Yuda nso rentan Efraim ani.
14 Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
Wobetwiw afa Filistia asiansian ahorow no so akɔ atɔe fam; na wɔbɛbɔ mu afow nnipa akɔ apuei fam. Wɔbɛfa Edom ne Moab, na Amonfo bɛhyɛ wɔn ase.
15 Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
Awurade bɛma nsu a ɛwɔ Misraim Po no mu ayow korakora; ɔbɛma ne nsa mu mframa a mu yɛ hyew abɔ afa Asubɔnten Eufrate so. Ɔbɛpaapae mu ayɛ no nsuwansuwa ason sɛnea ɛbɛyɛ a obiara betumi ahyɛ mpaboa atwa.
16 Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.
Ɔtempɔn bi bɛda hɔ ama ne nkurɔfo nkae a wɔaka Asiria, sɛnea bi daa hɔ maa Israel bere a wofi Misraim bae no.

< Yesaya 11 >