< Yesaya 26 >

1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
Saa da no, wɔbɛto saa dwom yi wɔ Yuda asase so: Yɛwɔ kuropɔn dennen; Onyankopɔn de nkwagye ayɛ nʼafasu ne ne hankare a ɛkorɔn.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Mummuebue apon no na atreneefo man no nhyɛn mu, ɔman nokwafo no.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
Wobɛkora no so asomdwoe mu nea wasi nʼadwene pi, efisɛ ɔde ne ho to wo so.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Fa wo ho to Awurade so afebɔɔ, efisɛ, Awurade, Awurade yɛ daa Botan.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
Ɔbrɛ wɔn a wɔtete soro ase, na ɔbrɛ kuropɔn a ɛkorɔn no ase; obubu gu fam pasaa ma ɛda mfutuma mu.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
Anammɔn tiatia so, wɔn a wɔhyɛ wɔn so anammɔn ahiafo anammɔntu.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
Ɔtreneeni kwan so yɛ tamaa; wo, Ɔnokwafo, woma ɔtreneeni kwan so yɛ trontrom.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Yiw, Awurade, yɛnam wo mmara kwan so yi, yɛretwɛn wo; na wo din ne ne kɛseyɛ yɛ nea yɛn koma pɛ.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
Me kra pere hwehwɛ wo anadwo; anɔpa nso me honhom ani gyina wo. Sɛ wʼatemmu ba asase yi so a, nnipa a wɔwɔ wiase sua treneeyɛ.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
Ɛwɔ mu sɛ wuyi adom adi kyerɛ amumɔyɛfo de, nanso wonsua treneeyɛ; na mpo atreneefo asase so no, wɔkɔ so yɛ bɔne na wommu Awurade kɛseyɛ.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Ao Awurade, wɔama wo nsa so kɔ soro, nanso wonhu. Ma wonhu wo mmɔdemmɔ wɔ wo nkurɔfo ho na ɛnhyɛ wɔn aniwu; ma ogya a wɔasɔ ama wʼatamfo no nhyew wɔn.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Awurade, woama yɛn asomdwoe; nea yɛatumi ayɛ nyinaa wo na woayɛ ama yɛn.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
Awurade yɛn Nyankopɔn, awuranom afoforo bi adi yɛn so, nanso wo din nko ara na yɛ kamfo.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
Afei wɔawuwu, na wɔnte ase bio; ahonhom a wɔafi mu no wɔrensɔre. Wotwee wɔn aso na wosɛee wɔn wɔama yɛn werɛ afi wɔn.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
Woama ɔman no ayɛ kɛse, Awurade; woama ɔman no ayɛ kɛse; woahyɛ wo ho anuonyam; woatrɛtrɛw asase no ahye nyinaa mu.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
Awurade, wofi ahohia mu baa wo nkyɛn; bere a wotwee wɔn aso no, na wontumi mmue wɔn ano mpo mmɔ mpae.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
Sɛnea ɔpemfo a awo aka no fi ɔyaw mu bukabukaw ne mu na osu no, saa ara na yɛyɛe wɔ wʼanim, Awurade.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
Yenyinsɛnee, yɛkyemee wɔ ɔyaw mu nanso yɛwoo mframa. Yɛamfa nkwagye amma asase so; wɔanwo nnipa amma asase so.
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
Nanso wʼawufo benya nkwa; wɔn nipadua bɛsɔre. Ma wɔn a wɔtete mfutuma mu no, nsɔre mfa anigye nteɛ mu. Mo bosu te sɛ anɔpa bosu; asase beyi nʼafunu apue.
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
Monkɔ, me nkurɔfo, monhyɛnhyɛn mo adan mu na montoto apon no mu; momfa mo ho nsie bere tiaa bi kosi sɛ nʼabufuwhyew ano bedwo.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
Hwɛ, Awurade refi nʼatenae abɛtwe nnipa a wɔte asase so aso wɔ wɔn bɔne ho. Asase bɛda mogya a wɔahwie agu no so no adi; ɔrentumi mfa nʼatɔfo nsie bio.

< Yesaya 26 >