< Hoseya 1 >
1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
The word of Yahweh which came unto Hosea son of Beeri, in the days of Uzziah, Jotham, Ahaz, Hezekiah, kings of Judah, —and in the days of Jeroboam son of Joash, king of Israel.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
The beginning of the word of Yahweh with Hosea, was, —that Yahweh said unto Hosea, Go take thee a woman of unchastity, and the children of unchastity, for, unchastely indeed, hath the land been going away from following Yahweh.
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
So he went and took Gomer, daughter of Diblaim, —and she conceived and bare him a son.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
Then said Yahweh unto him, Call his name Jezreel: for, yet a little, and I will visit the bloodshed of Jezreel upon the house of Jehu, and will cause to cease the kingdom of the house of Israel.
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
And it shall come to pass, in that day, that I will break the bow of Israel, in the vale of Jezreel.
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
Then conceived she again and bare a daughter, and he said to him, Call her name Lo-ruhamah ["Uncompassionated"], —for, not again any more, will I have compassion upon the house of Israel, that I should, forgive, them;
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
but, on the house of Judah, will I have compassion, and I will save them, as Yahweh their God, —but will not save them by bow, or by sword, or by battle, by horses, or by horsemen.
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
And, when she had weaned Lo-ruhamah, she conceived, and bare a son.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
Then said he, Call his name Lo-ammi ["No people of mine"], —for ye are Lo-ammi ["No people of mine"], and, I, will not be yours.
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
Yet shall the number of the sons of Israel become like the sand of the sea, which can neither he measured, nor numbered, —and it shall come to pass, in the place where it used to be said to them, No people of mine, are ye, it shall be said to them, Sons of a Living God!
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
Then shall the sons of Judah and the sons of Israel, gather themselves together, as one, and shall appoint them one head, and come up out of the earth, —for great shall be the day of Jezreel.