< Yeremiya 52 >

1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Twenty-one years old, was Zedekiah when he began to reign, and eleven years, reigned he, in Jerusalem, —and, his mother’s name, was Hamutal, daughter of Jeremiah of Libnah.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
And he did that which was wicked in the eyes of Yahweh, —according to all that Jehoiakim had done.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
For it was, because the anger of Yahweh, had come against Jerusalem and Judah until he had cast them out from his presence, that Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
And it came to pass in the ninth year of his reign, in the tenth month, on the tenth of the month, that Nebuchadrezzar king of Babylon came, he and all his force, against Jerusalem, and encamped against it, —and he built against it a siege-wall round about.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
And the city came into the siege, —until the eleventh year of King Zedekiah.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
In the fourth month on the ninth of the month, when the famine had become severe in the city, —and there had come to be no bread for the people of the land,
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
then was the city broken up, and all the men of war, beginning to flee went forth out of the city by night, by way of the gate between the two walls which was by the garden of the king the Chaldeans being near the city round about), —and they went the way towards the Waste Plain.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
And the force of the Chaldeans pursued the king, and overtook Zedekiah, in the Waste Plains of Jericho, —and, all his force, was scattered from him.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
So they seized the king, and brought him up, unto the king of Babylon at Riblah, in the land of Hamath, —and he pronounced upon him sentences of judgment.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
And the king of Babylon slew the sons of Zedekiah before his eyes, —moreover also all the princes of Judah, slew he in Riblah;
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
and the eyes of Zedekiah, put he out, —and bound him with fetters of bronze and the king of Babylon took him to Babylon, and put him in prison—until the day of his death.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
And in the fifth month on the tenth of the month, the same, was the nineteenth year of King Nebuchadrezzar, king of Babylon, came Nebuzaradan, chief of the royal executioners, —who stood before the king of Babylon into, Jerusalem;
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
and he burned the house of Yahweh and the house of the king, —yea all the houses of Jerusalem even every great man’s house, burned he with fire;
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
and all the walls of Jerusalem round about, did all the force of the Chaldeans who were with the chief of the royal executioners, break down.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
And some of the poor of the people and the residue of the people who were left in the city, and the disheartened who had fallen away unto the king of Babylon and the residue of the multitude, did Nebuzaradan chief of the royal executioners carry away captive.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
But, others of the poor of the land, did Nebuzaradan chief of the royal executioners leave, for vinedressers and for husbandmen.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
And the pillars of bronze that pertained to the house of Yahweh and the stands and the sea of bronze which was in the house of Yahweh, did the Chaldeans, break in pieces, —and they carried away all the bronze of them to Babylon;
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
and the caldrons and the shovels and the snuffers and the dashing bowls, and the spoons even all the utensils of bronze wherewith ministration used to be made did they take away;
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
and the basins and the censers and the dashing bowls and the caldrons and the lamps and the spoons and the cups, which were of gold in gold, and which were of silver in silver, did the chief of the royal executioners, take away.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
As for the two pillars the one sea, and the twelve oxen of bronze which were under the stands which King Solomon had made for the house of Yahweh, without weight was the bronze of all these things.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
Now as for the pillars, eighteen cubits, was the height of each pillar, and, a line of twelve cubits, compassed it about, —and the thickness thereof was four fingers’ breadth—hollow;
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
and there was, a capital, upon it, of bronze, and the height of each capital, was five cubits, with lattice-work and pomegranates upon the capital round about—the whole was of bronze, —and like these, were the second pillar and the pomegranates.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
And the pomegranates were ninety-six on a side, —all the pomegranates were a hundred upon the lattice-work round about.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
And the chief of the royal executioners, took away, Seraiah the first priest, and Zephaniah, the second priest, —and the three keepers of the entrance-hall;
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
and out of the city, took he one eunuch who was in charge over the men of war and seven men of them who used to watch the face of the king, who were found in the city, and the scribe of the prince of the host, who used to muster the people of the land, —and sixty men of the people of the land, who were found in the midst of the city.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
And when Nebuzaradan chief the royal executioners, had taken them, and brought them unto the king of Babylon at Riblah,
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
then did the king of Babylon smite them and put them to death at Riblah in the land of Hamath, —thus carried he Judah captive away from off their own soil.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
This, is the people, whom Nebuchadrezzar carried away captive, —In the seventh year—of them of Judah, three thousand and twenty-three;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
In the eighteenth year of Nebuchadrezzar—out of Jerusalem, eight hundred and thirty-two souls;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
In the three-and-twentieth year of Nebuchadrezzar, Nebuzaradan, chief of the royal executioners took away captive, of them of Judah, seven hundred and forty-five souls: All, the souls, were four thousand and six hundred.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
And it came to pass, in the thirty-seventh year of the captivity of Jehoiachin king of Judah, in the twelfth month, on the twenty-fifth of the month, that Evil-merodach king of Babylon, in the year he began to reign, lifted up, the head of Jehoiachin king of Judah, and brought him forth out of prison;
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
and spake with him comfortable words, —and set his throne above the throne of the kings who were with him in Babylon;
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
so he changed his prison garments, —and used to eat bread before his face continually, all the days of his life.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
And his allowance, was a continual allowance given him from the king of Babylon the portion of the day upon its own day, until the day of his death, —all the days of his life.

< Yeremiya 52 >