< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
A LAILA olelo mai la o Iehova ia'u, E hele hoi, e aloha aku i ka wahine i alohaia e ka hoalauna, aka, ke moe kolohe nae: E like me ke aloha o Iehova i na mamo a Iseraela, I ka poe e huli ana i na akua e, A e makemake hoi i na pai huawaina.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
A kuai aku la au ia ia na'u i na kala he umikumamalua a me ka homera a me ka hapalua o ka homera bale:
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
A i aku la au ia ia, E kali oe ia'u i na la he nui, Aole oe e hele i ka moe kolohe, Aole oe e lilo i ke kanaka e ae: Pela hoi e lilo ai au nau.
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
No ka mea, he nui na la e noho ai na mamo a Iseraela, aohe alii, aohe haku, aohe mohai, aohe kii, aohe epoda, aohe terapima:
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Mahope iho e huli mai na mamo a Iseraela, a imi ia Iehova ko lakou Akua, a me Davida ko lakou alii; A e makau lakou ia Iehova, a me kona lokomaikai i na la mahope.

< Hoseya 3 >