< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
Yahvé m'a dit: « Va encore, aime une femme aimée par un autre, une adultère, comme Yahvé aime les enfants d'Israël, bien qu'ils se tournent vers d'autres dieux et qu'ils aiment les gâteaux de raisins secs. »
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
Je l'achetai pour moi, pour quinze pièces d'argent et un homer et demi d'orge.
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
Je lui dis: « Tu resteras avec moi de nombreux jours. Tu ne te prostitueras pas, et tu ne seras pas avec un autre homme. J'agirai de même envers toi. »
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
Car les enfants d'Israël vivront longtemps sans roi, sans prince, sans sacrifice, sans pierre sacrée, sans éphod et sans idoles.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Ensuite, les enfants d'Israël reviendront et chercheront Yahvé, leur Dieu, et David, leur roi, et ils viendront avec tremblement à Yahvé et à ses bénédictions, dans les derniers jours.

< Hoseya 3 >