< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
La première année de Darius, fils d'Assuérus, de la descendance des Mèdes, qui fut établi roi sur le royaume des Chaldéens -
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
la première année de son règne, moi, Daniel, je compris par les livres le nombre des années au sujet desquelles la parole de Yahvé fut adressée à Jérémie, le prophète, pour l'accomplissement des désolations de Jérusalem, soit soixante-dix ans.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
Je me suis tourné vers le Seigneur Dieu, pour le consulter par des prières et des supplications, avec des jeûnes, des sacs et des cendres.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
J'ai prié Yahvé, mon Dieu, et je me suis confessé, en disant, « Seigneur, Dieu grand et redoutable, qui garde l'alliance et la bonté envers ceux qui l'aiment et gardent ses commandements,
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
nous avons péché, nous avons agi avec perversité, nous avons fait le mal, nous nous sommes rebellés, nous nous sommes détournés de tes préceptes et de tes ordonnances.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
Nous n'avons pas écouté tes serviteurs les prophètes, qui ont parlé en ton nom à nos rois, à nos princes, à nos pères et à tout le peuple du pays.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
« Seigneur, la justice t'appartient, mais à nous la confusion de visage, comme aujourd'hui, aux hommes de Juda, aux habitants de Jérusalem, et à tout Israël, proches et lointains, dans tous les pays où tu les as chassés, à cause de la faute qu'ils ont commise contre toi.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Seigneur, à nous la confusion du visage, à nos rois, à nos princes et à nos pères, parce que nous avons péché contre toi.
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
Au Seigneur notre Dieu appartiennent la miséricorde et le pardon, car nous nous sommes révoltés contre lui.
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
Nous n'avons pas obéi à la voix de l'Éternel, notre Dieu, pour marcher dans ses lois, qu'il nous avait prescrites par ses serviteurs les prophètes.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
Oui, tout Israël a transgressé ta loi, en se détournant, pour ne pas obéir à ta voix. « C'est pourquoi la malédiction et le serment écrits dans la loi de Moïse, serviteur de Dieu, ont été répandus sur nous, car nous avons péché contre lui.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
Il a confirmé les paroles qu'il a prononcées contre nous et contre les juges qui nous ont jugés, en faisant venir sur nous un grand malheur; car, sous tout le ciel, il n'a pas été fait à Jérusalem ce qui lui a été fait.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Comme il est écrit dans la loi de Moïse, tout ce malheur est venu sur nous. Et nous n'avons pas imploré la faveur de l'Éternel, notre Dieu, pour que nous nous détournions de nos iniquités et que nous soyons éclairés par ta vérité.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
C'est pourquoi l'Éternel a veillé sur le malheur et l'a fait venir sur nous; car l'Éternel, notre Dieu, est juste dans toutes les œuvres qu'il fait, et nous n'avons pas obéi à sa voix.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
« Maintenant, Seigneur notre Dieu, toi qui as fait sortir ton peuple du pays d'Égypte d'une main puissante, et qui t'es acquis une renommée, comme c'est le cas aujourd'hui, nous avons péché. Nous avons fait le mal.
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
Seigneur, selon toute ta justice, fais que ta colère et ton courroux se détournent de ta ville Jérusalem, ta montagne sainte, car à cause de nos péchés et des iniquités de nos pères, Jérusalem et ton peuple sont devenus un opprobre pour tous ceux qui nous entourent.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
« Maintenant, notre Dieu, écoute la prière de ton serviteur et ses supplications, et fais briller ta face sur ton sanctuaire dévasté, à cause du Seigneur.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Mon Dieu, tends l'oreille et écoute. Ouvre tes yeux et vois nos désolations, et la ville qui est appelée de ton nom; car nous ne présentons pas nos requêtes devant toi à cause de notre justice, mais à cause de tes grandes compassions.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Seigneur, écoute. Seigneur, pardonne. Seigneur, écoute et fais. Ne diffère pas, pour ton bien, mon Dieu, parce que ta ville et ton peuple sont appelés par ton nom. »
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
Pendant que je parlais, que je priais, que je confessais mon péché et le péché de mon peuple d'Israël, et que je présentais mes supplications à Yahvé mon Dieu pour la montagne sainte de mon Dieu -
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
oui, pendant que je parlais en priant - l'homme Gabriel, que j'avais vu dans la vision du début, se mit à voler rapidement et me toucha au moment de l'offrande du soir.
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
Il m'instruisit et s'entretint avec moi, et dit: « Daniel, je suis venu maintenant pour te donner la sagesse et l'intelligence.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
Au début de tes requêtes, le commandement est sorti, et je suis venu te le dire, car tu es très aimé. Considère donc la question et comprends la vision.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
« Soixante-dix semaines ont été décrétées pour ton peuple et pour ta ville sainte, afin d'achever la désobéissance, de faire cesser les péchés, de réparer l'iniquité, d'instaurer la justice éternelle, de sceller les visions et les prophéties, et d'oindre le Très Saint.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
« Sachez donc et discernez que, depuis l'envoi du commandement de rétablir et de reconstruire Jérusalem jusqu'à l'Oint, le prince, il y aura sept semaines et soixante-deux semaines. Elle sera rebâtie, avec des rues et des douves, même en des temps troublés.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
Après les soixante-deux semaines, l'Oint sera retranché et n'aura plus rien. Le peuple du prince qui vient détruira la ville et le sanctuaire. Sa fin sera un déluge, et la guerre durera jusqu'à la fin. Les désolations sont déterminées.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
Il conclura avec beaucoup de gens une alliance ferme pour une semaine. Au milieu de la semaine, il fera cesser le sacrifice et l'offrande. Sur l'aile des abominations viendra celui qui fait la désolation; et jusqu'au terme fixé, la colère se répandra sur les désolés. »

< Danieli 9 >