< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Return thou, O Israel, unto Yahweh thy God, —for thou hast stumbled by thine iniquity.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Take with you words, and return to Yahweh: say unto him—Wholly, shalt thou take away iniquity, Accept, then, with favour, and we will make good the boldness of our lips!
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assyria, shall not save us, Upon horses, will we not ride, neither will we say any more—Our god! to the work of our own hands! For, in thee, shall the fatherless, find compassion.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
I will heal their apostacy, I will love them freely, —for mine anger, hath turned, from them.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
I will become as the dew unto Israel, he shall break forth as the lily, —and he shall strike his roots as Lebanon:
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
His branches, shall spread, that, like an olive-tree, may be his fresh beauty, —and his fragrance, like Lebanon.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
They who dwell in his shade shall again show life like the corn, and break forth as the vine, —and, the remembrance of him, shall be like the wine of Lebanon.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ephraim [saith] —What to me any more are idols? I, have answered, and have closely observed him, I, am like a fir-tree that is green, From me, is thy fruit found.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Who is wise, that he may understand these things? intelligent, that he may take knowledge of them? For, straightforward, are the ways of Yahweh, and, the righteous, shall travel therein, but, transgressors, shall stumble therein.

< Hoseya 14 >