< Hoseya 11 >
1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
Кад Израиљ беше дете, љубих га, и из Мисира дозвах сина свог.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
Колико их зваше, толико они одлазише од њих; приносише жртве Валима, кадише ликовима.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Ја учих Јефрема ходити држећи га за руке, али не познаше да сам их ја лечио.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
Вукох их узицама човечијим, ужима љубавним; и бих им као они који им скидају јарам с чељусти, и давах им храну.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
Неће се вратити у земљу мисирску, него ће му Асирац бити цар, јер се не хтеше обратити.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
И мач ће стајати у градовима његовим, и потрће преворнице његове и прождрети за намере њихове.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
Народ је мој прионуо за отпад од мене; зову га ка Вишњем, али се ниједан не подиже.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
Како да те дам, Јефреме? Да те предам, Израиљу? Како да учиним од тебе као од Адаме? Да те обратим да будеш као Севојим? Устрептало је срце моје у мени, усколебала се утроба моја од жалости.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
Нећу извршити љутог гнева свог, нећу опет затрти Јефрема; јер сам ја Бог а не човек, Светац усред тебе; нећу доћи на град.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
Ићи ће они за Господом; Он ће рикати као лав; кад рикне, са страхом ће дотрчати синови с мора;
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
Са страхом ће дотрчати из Мисира као птица, и као голуб из земље асирске; и населићу их у кућама њиховим, говори Господ.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Опколио ме је Јефрем лажју и дом Израиљев преваром; али Јуда још влада с Богом и веран је са светима.