< Hoseya 10 >

1 Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
Израиљ је празна лоза винова, оставља род за се; што више рода има, то више умножава олтаре; што му је боља земља, то више кити ликове.
2 Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
Срце им је раздељено, зато су криви; Он ће оборити олтаре њихове, поломиће ликове њихове.
3 Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
Јер сада говоре: Немамо цара; не бојимо се Господа; и шта би нам учинио цар?
4 Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
Говоре речи кунући се лажно кад уговарају веру, и суд као отров расте у браздама на њиви мојој.
5 Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
За јунице вет-авенске уплашиће се становници самаријски; јер ће за њима жалити народ њихов, и свештеници њихови, који им се радоваху, јер ће слава њихова отићи од њих.
6 Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
И он ће сам бити одведен у Асирску на дар цару браничу; Јефрема ће попасти стид, и Израиљ ће се осрамотити намером својом.
7 Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
Цара ће самаријског нестати као пене поврх воде.
8 Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
И обориће се висине авенске, грех Израиљев; трње ће и чкаљ расти по олтарима њиховим, и говориће горама: Покријте нас, и хумовима: Падните на нас.
9 “Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
Од времена гавајског грешио си, Израиљу; онде осташе, не стиже их у Гаваји рат на безаконике.
10 Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
По својој ћу их вољи покарати, и народи ће се скупити на њих да их заробе за двојако безакоње њихово.
11 Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
Јефрем је јуница научена, која радо врше; али ћу јој доћи на лепи врат; упрегнућу Јефрема, Јуда ће орати, Јаков ће повлачити.
12 Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
Сејте правду, жећете милост; орите крчевину, јер је време да тражите Господа, да би дошао и подаждио вам правдом.
13 Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
Орасте безбожност, жесте безакоње, једосте плод од лажи; јер си се поуздао у свој пут, у мноштво својих јунака.
14 phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
Зато ће се подигнути врева међу твојим народом, и сви ће се градови твоји раскопати као што Салман раскопа Вет-Арвел кад беше рат, мајка би размрскана са синовима.
15 Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.
Тако ће вам учинити Ветиљ за велику злоћу вашу; зором ће погинути цар Израиљев.

< Hoseya 10 >