< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
Then Jacob lifted up his feet and went unto the land of the children of the east.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
And he looked, and behold there was a well in the field, and, lo, there were three flocks of sheep lying by it; for out of that well they watered the flocks: and the stone upon the mouth of the well was great.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
And there all the flocks were wont to assemble; and they rolled then the stone from the mouth of the well, and watered the sheep; and they put the stone again upon the mouth of the well in its place.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
And Jacob said unto them, My brethren, whence are ye? And they said, Of Charan are we.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
And he said unto them, Know ye Laban the son of Nachor? And they said, We know him.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
And he said unto them, Is he well? And they said, He is well; and, behold, Rachel his daughter cometh with the sheep.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
And he said, Lo, the day is yet long, it is not time that the cattle should be driven home; water ye the sheep, and go and feed them.
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
And they said, We cannot, until all the flocks be gathered together, then do they roll the stone from the mouth of the well; and we water the sheep.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
And while he was yet speaking with them, Rachel came with her father's sheep; for she was a shepherdess.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
And it came to pass when Jacob saw Rachel the daughter of Laban his mother's brother, and the sheep of Laban his mother's brother, that Jacob went near, and rolled the stone from the mouth of the well, and watered the flock of Laban his mother's brother.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
And Jacob kissed Rachel, and lifted up his voice, and wept.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
And Jacob told Rachel that he was her father's brother, and that he was Rebekah's son: and she ran and told her father.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
And it came to pass, when Laban heard the tidings of Jacob his sister's son, that he ran to meet him, and embraced him, and kissed him, and brought him to his house. And he told Laban all these things.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
And Laban said to him, Surely thou art my bone and my flesh. And he abode with him the space of a month.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
And Laban then said unto Jacob, Because thou art my brother, shouldst thou therefore serve me for naught? tell me, what shall thy wages be?
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
And Laban had two daughters; the name of the elder was Leah, and the name of the younger was Rachel.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
And the eyes of Leah were tender; but Rachel was of handsome form and handsome appearance.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
And Jacob loved Rachel; and he said, I will serve thee seven years for Rachel thy younger daughter.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
And Laban said, It is better that I give her to thee, than that I should give her to another man; abide with me.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
And Jacob served for Rachel seven years; and they seemed unto him but a few days, through the love he had to her.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
And Jacob said unto Laban, Give me my wife, for my days are fulfilled, that I may go in unto her.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
And Laban gathered together all the men of the place, and made a feast.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
And it came to pass in the evening, that he took Leah his daughter, and brought her to him; and he went in unto her.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
And Laban gave unto his daughter Leah, Zilpah his maid for a handmaid.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
And it came to pass that in the morning, behold, it was Leah: and he said to Laban, What is this thou hast done unto me? did I not serve with thee for Rachel? wherefore then hast thou deceived me?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
And Laban said, It is not done so in our place, to give in marriage the younger before the first-born.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Fulfill the week of this, and we will give thee this one also, for the service which thou shalt serve with me yet seven other years.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
And Jacob did so, and fulfilled the week of the first; and he gave him Rachel his daughter for a wife.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
And Laban gave to Rachel his daughter Bilhah his hand-maid to be her maid.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
And he went in also unto Rachel, and he loved also Rachel more than Leah; and he served with him yet seven other years.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
And when the Lord saw that Leah was hated, he opened her womb; but Rachel was barren.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
And Leah conceived, and bore a son, and she called his name Reuben; for she said, Surely, the Lord hath looked upon my affliction, because now my husband will love me.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
And she conceived again and bore a son; and she said, Because the Lord heard that I was hated, he hath given me this one also; and she called his name Simeon.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
And she conceived again, and bore a son; and she said, Now this time will my husband be joined unto me, because I have born him three sons; therefore was his name called Levi.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
And she conceived again, and bore a son; and she said, This time will I praise the Lord; therefore she called his name Judah: and she left off bearing.

< Genesis 29 >