< Genesis 28 >

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
And Isaac called Jacob, and blessed him, and charged him, and said unto him, Thou shalt not take a wife from the daughters of Canaan.
2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
Arise, go to Padan-aram, to the house of Bethuel thy mother's father; and take thyself from there a wife of the daughters of Laban thy mother's brother.
3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
And God, the Almighty, bless thee, and make thee fruitful, and multiply thee, that thou mayest become a multitude of people;
4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
And may he give thee the blessing of Abraham, to thee, and to thy seed with thee; that thou mayest inherit the land of thy sojourn, which God gave unto Abraham.
5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
And Isaac sent away Jacob, and he went to Padan-aram, unto Laban, the son of Bethuel the Syrian, the brother of Rebekah, the mother of Jacob and Esau.
6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
And when Esau saw that Isaac had blessed Jacob, and sent him away to Padan-aram, to take himself from there a wife; and in blessing him had given him a charge, saying, Thou shalt not take a wife of the daughters of Canaan;
7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
And that Jacob had obeyed his father and his mother, and was gone to Padan-aram:
8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
Then saw Esau that the daughters of Canaan were evil in the eyes of Isaac his father;
9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
And Esau went unto Ishmael, and took Machalath the daughter of Ishmael, Abraham's son, the sister of Nebayoth in addition to his wives, to himself as wife.
10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
And Jacob went out from Beer-sheba, and went toward Charan.
11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
And he lighted upon a certain place, and tarried there all night, because the sun was set; and he took one of the stones of the place, and put it for his pillow, and laid himself down in that place.
12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
And he dreamed, and behold a ladder was set up on the earth, and the top of it reached to heaven; and behold, angels of God were ascending and descending on it.
13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
And, behold, the Lord stood above it, and said, I am the Lord, the God of Abraham thy father, and the God of Isaac: the land whereon thou liest, to thee will I give it, and to thy seed;
14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
And thy seed shall be as the dust of the earth, and thou shalt spread abroad to the west, and to the east, and to the north and to the south; and in thee and thy seed shall all the families of the earth be blessed.
15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
And, behold, I am with thee, and will keep thee whithersoever thou goest, and will bring thee again into this land; for I will not leave thee, until I have done what I have spoken to thee of.
16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
And Jacob awakened out of his sleep, and he said, Surely the Lord is present in this place; and I knew it not.
17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
And he was afraid, and said, How fearful is this place! this is none other but the house of God, and this is the gate of heaven.
18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
And Jacob rose up early in the morning, and took the stone that he had put for his pillow, and set it up for a pillar, and poured oil upon the top of it.
19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
And he called the name of that place Beth-el; but Luz was the name of that city in former times.
20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
And Jacob made a vow, saying, If God will be with me, and will keep me on this way which I am going, and will give me bread to eat, and raiment to put on,
21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
And I come again in peace to my father's house: then shall the Lord be my God;
22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”
And this stone, which I have set for a pillar, shall be God's house; and of all that thou wilt give me I will surely give the tenth unto thee.

< Genesis 28 >