< Genesis 2 >

1 Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
Tako sta bila končana nebo in zemlja in vsa njuna vojska.
2 Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
[7. dan] Na sedmi dan je Bog končal svoje delo, ki ga je naredil; in na sedmi dan je počival od vsega svojega dela, ki ga je naredil.
3 Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
Bog je blagoslovil sedmi dan ter ga posvetil, zato ker je na ta [dan] počival od vsega svojega dela, ki ga je Bog ustvaril in naredil.
4 Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
To so rodovi neba in zemlje, ko so bili ustvarjeni, na dan, ko je Gospod Bog naredil zemljo in nebo
5 zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
in vsako poljsko rastlino, preden je bila na zemlji in vsako poljsko zelišče, preden je zraslo, kajti Gospod Bog na zemljo ni poslal dežja in ni bilo človeka, da obdeluje tla.
6 koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
Toda meglica se je dvigala iz zemlje in namakala celotno obličje tal.
7 Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
Gospod Bog je iz prahu tal oblikoval človeka in v njegove nosnice vdihnil dih življenja, in človek je postal živa duša.
8 Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
Gospod Bog je zasadil vrt proti vzhodu v Edenu in tja je postavil človeka, ki ga je oblikoval.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
Gospod Bog je naredil, da iz tal požene vsako drevo, ki je prijetno pogledu in dobro za hrano; tudi drevo življenja v sredi vrta in drevo spoznanja dobrega in zla.
10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
In reka je izvirala iz Edena, da namaka vrt in od tam je bila razdeljena v štiri glave.
11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
Ime prve je Pišón. To je ta, ki obkroža celotno deželo Havilá, kjer je zlato
12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
in zlato te dežele je dobro; tam je bdelij in kamen oniks.
13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
Ime druge reke je Gihon. Ta ista je ta, ki obkroža celotno deželo Etiopijo.
14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
Ime tretje reke je Hidekel. To je ta, ki gre proti vzhodu Asirije. In četrta reka je Evfrat.
15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
Gospod Bog je vzel človeka ter ga postavil v edenski vrt, da ga prirezuje in da ga varuje.
16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
Gospod Bog je človeku zapovedal, rekoč: »Od vsakega vrtnega drevesa lahko prosto ješ,
17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
toda od drevesa spoznanja dobrega in zla, ne smeš jesti od njega, kajti na dan, ko boš od njega jedel, boš zagotovo umrl.«
18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
Gospod Bog je rekel: » To ni dobro, da bi bil človek sam. Naredil mu bom pomoč, primerno zanj.«
19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
Iz tal je Gospod Bog oblikoval vsako poljsko žival in vsako zračno perjad in jih privedel k Adamu, da vidi, kako jih bo poimenoval. In kakorkoli je Adam vsako živo ustvarjeno bitje poimenoval, to je bilo njeno ime.
20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
Adam je dal imena vsej živini, zračni perjadi in vsaki poljski živali, toda za Adama ni bilo najti pomoči, primerne zanj.
21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
Gospod Bog je storil, da je na Adama padlo globoko spanje in je zaspal. Vzel je eno izmed njegovih reber ter namesto le-tega zaprl meso
22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
in [iz] rebra, ki ga je Gospod Bog vzel iz človeka, je naredil žensko in jo privedel k človeku.
23 Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
Adam je rekel: »To je sedaj kost iz mojih kosti in meso iz mojega mesa. Imenovala se bo Ženska, ker je bila vzeta iz Moškega.«
24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
Zatorej bo moški zapustil svojega očeta in svojo mater in se bo trdno pridružil svoji ženi in oba bosta eno meso.
25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
Oba sta bila naga, mož in njegova žena in ni ju bilo sram.

< Genesis 2 >