< Genesis 18 >
1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
Gospod se mu je prikazal na Mamrejevih ravninah, on pa je sedel pri šotorskih vratih, v vročini dneva
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
in povzdignil svoje oči in pogledal in glej, pri njem so stali trije možje in ko jih je zagledal, je stekel od šotorskih vrat, da jih sreča in se priklonil proti tlom
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
ter rekel: »Moj Gospod, če sem torej našel naklonjenost v tvojih očeh, te prosim, ne odidi proč od svojega služabnika.
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Naj bo prineseno, prosim te, malo vode in umijte svoja stopala in se spočijte pod drevesom.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
Prinesel bom grižljaj kruha in potolažite svoja srca. Nató boste šli dalje, kajti zato ste prišli k svojemu služabniku.« In rekli so: »Stôri tako, kakor si rekel.«
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
Abraham se je podvizal v šotor k Sari ter ji rekel: »Brž pripravi tri mere fino mlete moke, zamesi jo in na ognjišču pripravi kolače.«
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
Abraham je stekel k čredi, vzel nežno in dobro tele ter ga dal mladeniču in ta je pohitel, da ga pripravi.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
Vzel je maslo, mleko in tele, ki ga je pripravil in to postavil prednje, in stal je poleg njih, pod drevesom, oni pa so jedli.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
Rekli so mu: »Kje je tvoja žena Sara?« Rekel je: »Glejte, v šotoru.«
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
In on je rekel: »Zagotovo se bom vrnil k tebi glede na čas življenja in glej, tvoja žena Sara bo imela sina.« Sara pa je to slišala pri vratih šotora, ki je bil za njim.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
Torej Abraham in Sara sta bila stara in zelo zvrhana v letih in s Saro je prenehalo biti po običaju žensk.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
Zato se je Sara v sebi zasmejala, rekoč: »Bom še imela užitek, potem ko sem se postarala [in] je tudi moj gospod postal star?«
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
Gospod je rekel Abrahamu: »Zakaj se je Sara zasmejala, rekoč: ›Bom zares rodila otroka jaz, ki sem stara?‹
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Je za Gospoda katerakoli stvar pretežka? Ob določenem času se bom vrnil k tebi, glede na čas življenja in Sara bo imela sina.«
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
Potem je Sara zanikala, rekoč: »Nisem se zasmejala, « kajti bila je prestrašena. On pa je rekel: »Ne, toda zasmejala si se.«
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
Možje so vstali od tam in pogledali proti Sódomi in Abraham je odšel z njimi, da jih pospremi na pot.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
Gospod je rekel: »Mar naj pred Abrahamom prikrijem to stvar, ki jo počnem,
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
glede na to, da bo Abraham zagotovo postal velik in mogočen narod in bodo v njem blagoslovljeni vsi narodi zemlje?
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Kajti poznam ga, da bo ukazal svojim otrokom in svoji družini za njim in se bodo držali Gospodove poti, da izvajajo pravičnost in sodbo, da bo Gospod nad Abrahama lahko privedel to, kar je govoril o njem.«
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
Gospod je rekel: »Ker je vpitje Sódome in Gomóre veliko in ker je njihov greh zelo boleč,
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
bom torej šel dol in pogledal, ali so storili povsem glede na njihovo vpitje, ki je prišlo do mene; in če ne, bom vedel.«
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
Možje so svoje obraze obrnili od tam in odšli proti Sódomi, toda Abraham je kljub temu stopil pred Gospoda.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
Abraham se je približal in rekel: »Hočeš prav tako uničiti pravične z zlobnimi?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Morda je znotraj mesta petdeset pravičnih. Hočeš prav tako uničiti kraj in mu ne prizanesti zaradi petdesetih pravičnih, ki so v njem?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
To bodi daleč od tebe, da storiš na ta način, da z zlobnimi pokončaš pravične in da bi bili pravični kakor zlobni, to bodi daleč od tebe. Mar ne bo Sodnik vse zemlje storil pravično?«
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
Gospod je rekel: »Če najdem v Sódomi, znotraj mesta, petdeset pravičnih, potem bom zaradi njih prizanesel celemu kraju.«
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
Abraham pa je odgovoril in rekel: »Glej torej, nase, ki sem samo prah in pepel, sem vzel, da govorim Gospodu.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Morda jih bo manjkalo pet do petdesetih pravičnih. Hočeš mesto uničiti zaradi pomanjkanja petih?« On pa je rekel: »Če jih najdem tam petinštirideset, ga ne bom uničil.«
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
Ponovno mu je spregovoril in rekel: »Morda jih bo tam najdenih štirideset.« On pa je rekel: » Tega ne bom storil zaradi štiridesetih.«
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
Rekel mu je: »Oh naj moj Gospod ne bo jezen, jaz pa bom govoril: ›Morda jih bo tam najdenih trideset.‹« On pa je rekel: » Tega ne bom storil, če jih tam najdem trideset.«
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
Rekel je: »Glej torej, vzel sem nase, da govorim Gospodu: ›Morda jih bo tam najdenih dvajset.‹« On pa je rekel: »Ne bom ga uničil zaradi dvajsetih.«
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
Rekel je: »Oh naj Gospod ne bo jezen, jaz pa bom govoril samo še tokrat: ›Morda jih bo tam najdenih deset.‹« On pa je rekel: »Ne bom ga uničil zaradi desetih.«
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
Gospod je odšel svojo pot takoj, ko je prenehal govoriti z Abrahamom. Abraham pa se je vrnil na svoj kraj.