< Agalatiya 6 >
1 Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe.
Ta ishato isi uray nagara oothi betiko inte qase ayanan loo7o dizayti iza ashaketethara zaranas beses gido attiin nekka izademala paccetonta mala ne hu7es nagista.
2 Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu.
Isay isa dexxo toho toko hessamalan oothon Kirstossa wogga pollista.
3 Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha.
Isadey ayne hanonta dishe ayko giitaso gakida milatiko he uray berika bena balethes.
4 Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake,
Isi isi uray ba ootho berika pacci xelo. Hesafe guye hara urara bena ginasonta diisheizi bena ceqisizaz demana.
5 pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
Isi isi uray berka ba toho tokanas beses.
6 Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
Qala tamarizay onika ba tamarida loo7o misha ba astamarera gishetes.
7 Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa.
Baletofite Xoosi qlicca erena. Assi ba zeridaro iza zera buccana.
8 Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios )
Be asho amo kunthanas zerizadey ashope dhaysi buccana. Ayana ufaysanas zeridadey gidiko ayanape medhina deyo buccana. (aiōnios )
9 Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa.
Ane nu loo7o ootho oothanas azaloko nu ufaysi qanxonta agiko wodey gakishin nu gakida kaatha maxana.
10 Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
Hesa gish loo7o ootho oothanas azaloko nu ufaysi qanxxonta agiko wodey gakiishin nu gakiida kaatha maxana.
11 Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
Tani ta kushera intes aymala gita piidalen xafidakone ane xeliite.
12 Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu.
Co kare bagara bistana koyza asati inte qaxaristanamala gidesana koyetes. Isti hessa oothzay Kirstossa masqale gish gidi godetonta malako.
13 Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo.
Isti inte qaxaristanamala koyzay inte ashon ceeqistanas koyza gish attiin qaxaretidayti Muse wogga nagizayta gidetena.
14 Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi.
Qase 7alamey tas taka 7alames kaqetida Goda Yesuss Kiristossa masqalepe attiin hara ceqoy tape hakko.
15 Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano.
Qaxaretin woykko qaxaretonta agin izas go7ay bawa. Go7ay medheteth.
16 Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
Haysa ha azazoza kaalliza wurisosine Xoossa dere gidida Isra7elistas saroyne marotethi gido.
17 Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
Tani Yesussa malata ta asatethan tokadis hessa gish hi7a tana oonikka waysena.
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
Ta ishato Goda Yesus Kiristossa adho kiyatethi intenara godo. Amiini