< Ezara 5 >
1 Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
O sırada Peygamber Hagay ile İddo oğlu Peygamber Zekeriya, Yahuda ve Yeruşalim'deki Yahudiler'e İsrail Tanrısı'nın adıyla peygamberlikte bulundular.
2 Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
Bunun üzerine Şealtiel oğlu Zerubbabil ile Yosadak oğlu Yeşu Tanrı'nın Yeruşalim'deki Tapınağı'nı yeniden kurmaya giriştiler. Tanrı'nın peygamberleri de onlarla birlikteydi ve onlara yardım ediyordu.
3 Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
Fırat'ın batı yakasındaki bölgenin valisi Tattenay, Şetar-Bozenay ve çalışma arkadaşları onlara gidip, “Bu tapınağı yeniden kurmak ve yapımını tamamlamak için size kim yetki verdi?” diye sordular.
4 Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
Yapıyı kuranların adlarını da sordular.
5 Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
Ama Tanrıları Yahudi ileri gelenlerini koruyordu. Bu yüzden, Darius'a bir haber gönderilip ondan yazılı bir yanıt alınıncaya dek Yahudiler durdurulmadı.
6 Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
Fırat'ın batı yakasındaki bölgenin valisi Tattenay, Şetar-Bozenay, çalışma arkadaşları ve oradaki görevlilerin Kral Darius'a gönderdikleri mektubun örneği aşağıdadır.
7 Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
Gönderdikleri belge şöyleydi: “Kral Darius'a candan selamlar.
8 Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
Yahuda İli'ne, yüce Tanrı'nın Tapınağı'na gittiğimizi krala bildiririz. Tapınağı büyük taşlarla kuruyor, duvarlarına kirişler yerleştiriyorlar. Tapınağın yapımında canla başla çalışılıyor ve yapım işi başarıyla ilerliyor.
9 Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
“Halkın ileri gelenlerine, ‘Bu tapınağı yeniden kurmak ve yapımını tamamlamak için size kim yetki verdi?’ diye sorduk.
10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
Bilgine sunmak üzere önderlerinin kim olduklarını sana yazabilmek için adlarını da sorduk.
11 Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
“İşte bize verdikleri yanıt: “‘Biz yerin ve göğün Tanrısı'nın kullarıyız. Uzun yıllar önce İsrail'in büyük bir kralının kurup yapımını tamamladığı tapınağı yeniden kuruyoruz.
12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Ama atalarımız Göklerin Tanrısı'nı öfkelendirdi. Bu yüzden Tanrı onları Babil Kralı Kildani Nebukadnessar'ın eline teslim etti. Nebukadnessar tapınağı yıktı, halkı da Babil'e sürdü.
13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
Ama Babil Kralı Koreş, krallığının birinci yılında Tanrı'nın Tapınağı'nın yeniden yapılması için buyruk verdi.
14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
Ayrıca Nebukadnessar'ın Tanrı'nın Yeruşalim'deki Tapınağı'ndan çıkarıp Babil'deki tapınağa götürdüğü altın ve gümüş kapları da oradan çıkararak vali atadığı Şeşbassar adlı kişiye verdi.
15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
Koreş ona, Bu kapları al, gidip Yeruşalim'deki tapınağa yerleştir dedi, Tanrı'nın Tapınağı'nı eski yerinde yeniden kur.
16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
Böylece Şeşbassar gelip Tanrı'nın Yeruşalim'deki Tapınağı'nın temelini attı. O günden bu yana yapım işleri sürmekte, ama daha bitmedi.’
17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.
“Kral uygun görüyorsa, Babil Sarayı'ndaki arşivde bir araştırma yapılsın. Tanrı'nın Yeruşalim'deki Tapınağı'nın yeniden kurulması için Kral Koreş'in bir buyruk verip vermediği saptansın. Sonra kral bu konuya ilişkin kararını bize bildirsin.”