< 2 Mbiri 1 >

1 Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
Davut oğlu Süleyman krallığını sağlamlaştırdı. Çünkü Tanrısı RAB onunlaydı ve onu çok yüceltti.
2 Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
Süleyman bütün İsrailliler'i –binbaşıları, yüzbaşıları, yargıçları, İsrail'in boy başları olan önderleri– çağırttı.
3 Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
Sonra bütün toplulukla birlikte Givon'daki tapınma yerine gitti. Çünkü RAB'bin kulu Musa'nın çölde yaptığı Tanrı'yla Buluşma Çadırı oradaydı.
4 Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
Ancak Davut Tanrı'nın Antlaşma Sandığı'nı Kiryat-Yearim'den getirip Yeruşalim'de hazırladığı çadıra koymuştu.
5 Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
Hur oğlu Uri oğlu Besalel'in yaptığı tunç sunağı da Givon'da RAB'bin Konutu'nun önüne yerleştirmişti. Süleyman'la topluluk orada RAB'be danıştılar.
6 Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
Süleyman RAB'bin önüne, Buluşma Çadırı'nın önündeki tunç sunağa çıkarak üzerinde bin yakmalık sunu sundu.
7 Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
Tanrı o gece Süleyman'a görünüp, “Sana ne vermemi istersin?” diye sordu.
8 Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Süleyman, “Babam Davut'a büyük iyilikler yaptın” diye karşılık verdi, “Beni de onun yerine kral atadın.
9 Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
Ya RAB Tanrı, babam Davut'a verdiğin söz yerine gelsin! Beni yeryüzünün tozu kadar çok olan bir halkın kralı yaptın.
10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Şimdi bu halkı yönetebilmem için bana bilgi ve bilgelik ver. Başka türlü senin bu büyük halkını kim yönetebilir!”
11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
Tanrı Süleyman'a, “Demek yüreğinin dileği bu” dedi, “Zenginlik, mal mülk, onur ya da senden nefret edenlerin ölümünü istemedin, kendin için uzun ömür de istemedin. Bunların yerine seni başına kral yaptığım halkımı yönetmek için bilgi ve bilgelik istedin.
12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
Sana bilgi ve bilgelik verilecektir. Sana ayrıca öyle bir zenginlik, mal mülk ve onur vereceğim ki, benzeri ne senden önceki krallarda görülmüştür, ne de senden sonrakilerde görülecektir.”
13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
Bundan sonra Süleyman Givon'daki tapınma yerinden, Buluşma Çadırı'ndan ayrılıp Yeruşalim'e gitti. İsrail'i oradan yönetti.
14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
Kral Süleyman savaş arabalarıyla atlarını topladı. Bin dört yüz savaş arabası, on iki bin atı vardı. Bunların bir kısmını savaş arabaları için ayrılan kentlere, bir kısmını da kendi yanına, Yeruşalim'e yerleştirdi.
15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
Krallığı döneminde Yeruşalim'de altın ve gümüş taş değerine düştü. Sedir ağaçları Şefela'daki yabanıl incir ağaçları kadar bollaştı.
16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
Süleyman'ın atları Mısır ve Keve'den getirilirdi. Kralın tüccarları atları Keve'den satın alırdı.
17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.
Mısır'dan bir savaş arabası altı yüz, bir at yüz elli şekel gümüşe getirilirdi. Bunları bütün Hitit ve Aram krallarına satarlardı.

< 2 Mbiri 1 >