< Ezekieli 6 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
„Фиул омулуй, ынтоарче-ць фаца спре мунций луй Исраел, пророчеште ымпотрива лор
3 kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
ши зи: ‘Мунць ай луй Исраел, аскултаць кувынтул Домнулуй Думнезеу! Аша ворбеште Домнул Думнезеу, кэтре мунць ши дялурь, кэтре вэгэунь ши вэй: «Ятэ, вой адуче сабия ымпотрива воастрэ ши вэ вой нимичи ынэлцимиле.
4 Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
Алтареле воастре вор фи пустиите, стылпий воштри ынкинаць соарелуй вор фи сфэрымаць ши вой фаче ка морций воштри сэ кадэ ынаинтя идолилор воштри.
5 Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
Вой пуне трупуриле моарте але копиилор луй Исраел ынаинтя идолилор лор ши вэ вой рисипи оаселе ын журул алтарелор воастре.
6 Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
Претутиндень пе унде локуиць, четэциле вэ вор фи нимичите ши ынэлцимиле, пустиите; алтареле воастре вор фи сурпате ши пэрэсите, идолий воштри вор фи сфэрымаць ши вор пери, стылпий воштри ынкинаць соарелуй вор фи тэяць ши лукрэриле воастре, нимичите.
7 Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
Морций вор кэдя ын мижлокул востру ши вець шти кэ Еу сунт Домнул.
8 “Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
Дар вой лэса кытева рэмэшице динтре вой, каре вор скэпа де сабие принтре нямурь кынд вець фи рисипиць ын фелурите цэрь.
9 Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
Ши чей че вор скэпа дин вой ышь вор адуче аминте де Мине принтре нямуриле унде вор фи робь, пентру кэ ле вой здроби инима прякурварэ ши некрединчоасэ ши окий каре ау курвит дупэ идолий лор. Атунч ле ва фи скырбэ де ей ыншишь дин причина мишелиилор пе каре ле-ау фэкут, дин причина тутурор урычунилор лор.
10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул ши кэ ну деӂяба й-ам аменинцат кэ ле вой тримите тоате ачесте реле.»
11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Бате дин мынь, дэ дин пичоаре ши зи: ‹Вай! пентру тоате урычуниле челе реле але касей луй Исраел, каре ва кэдя ловитэ де сабие, де фоамете ши де чумэ.
12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
Чине ва фи департе ва мури де чумэ ши чине ва фи апроапе ва кэдя учис де сабие, яр чине ва рэмыне ши ва фи ымпресурат ва пери де фоаме. Аша Ымь вой потоли урӂия асупра лор.
13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
Ши вець шти кэ Еу сунт Домнул кынд морций лор вор фи ын мижлокул идолилор лор, ымпрежурул алтарелор лор, пе орьче дял ыналт, пе тоате вырфуриле мунцилор, суб орьче копак верде, суб орьче стежар стуфос, аколо унде адучяу тэмые ку мирос плэкут тутурор идолилор лор.
14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Ымь вой ынтинде мына ымпотрива лор ши вой фаче цара дешартэ ши пустие, де ла пустиу пынэ ла Дибла, претутиндень унде локуеск. Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул.›»’”

< Ezekieli 6 >