< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
Then he brought me back toward the outer gate of the sanctuary, which looked toward the east, —but, it was shut.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
Then said Yahweh unto me This gate shut, shall remain It shall not be opened And no man shall enter thereby, Because Yahweh, God of Israel, doth enter thereby, - Therefore shall it remain—shut.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
The prince! as prince, he, shall sit therein, To eat food before Yahweh, — By way of the porch of the gate, shall he go in, and By way thereof, shall he come out.
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
Then he brought me in by way of the north gate unto the front of the house, and I looked and lo! the glory of Yahweh, filled the house of Yahweh, — so I fell upon my face.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
And Yahweh said unto me, Son of man Apply thy heart And see with thine eyes And with thine ears, hear thou All that I am speaking with thee, As to all the statutes of the house of Yahweh and As to all the laws thereof, - And thou shalt apply thy heart To the entering in of the house, With all the exits of the sanctuary.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
So then thou shalt say unto the perverse [house] unto the house of Israel, Thus saith My Lord, Yahweh: Let it more than suffice you Out of all your abominations, O house of Israel:
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
That ye brought in the sons of the foreigner Uncircumcised in heart and uncircumcised in flesh, To be in my sanctuary. So that he profaned my house, - That ye brought near as my food the fat and the blood, And so they brake my covenant—Among all your abominations;
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
Neither kept ye the charge of my holy things, - But ye did set men to be keepers of my charge in my sanctuary, for your own pleasure,
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Thus saith My Lord, Yahweh, No son of a foreigner Uncircumcised in heart and uncircumcised in flesh, shall enter into my sanctuary, —of any son of a foreigner, who is in the midst of the sons of Israel.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
But as for the Levites. Who went far from me, when Israel went astray. Who went astray from me, after their manufactured gods, Therefore shall they bear their iniquity,
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
Yet shall they remain in my sanctuary As attendants in charge at the gates of the house, — And attending upon the house, — They shall slay the ascending-offering, and the sacrifice of the people, And they, shall stand before them to wait upon them.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Because they used to wait upon them before their manufactured gods, and became to the house of Israel a stumbling-block of iniquity, For this cause have I lifted up my hand concerning them Declareth My Lord Yahweh, and they shall bear their iniquity;
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
So then they shall not come near unto me To minister as priests unto me, Nor come near unto any of my holy things, As regardeth things most holy, — But they shall bear their rebuke, and their abominations which they have committed;
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
Yet will I make them keepers of the charge of the house, — As to all the labour thereof, and As to all which shall be done therein.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
But the priests the Levites the sons of Zadok, Who kept the charge of my sanctuary— when the sons of Israel went astray from me, They shall draw near unto me to wait upon me, And shall stand before me, to bring near unto me the fat and the blood Declareth My Lord, Yahweh:
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
They shall enter into my sanctuary, and They shall draw near unto my table to wait upon me, - So shall they keep my charge.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
And it shall be when they shall enter into the gates of the inner court, Garments of linen, shall they put on, Yea there shall come upon them no wool, when they minister in the gates of the inner court and within:
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
Chaplets of linen, shall be upon their head, and Breeches of linen shall be upon their loins, — They shall not gird themselves, so as to perspire,
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
And when they go forth into the outer court into the outer court unto the people, They shall put off their garments, wherein they do minister, and lay them in the chambers of the holy place, - And shall put on other garments, That they may not hallow the people by their garments.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
And their heads, shall they not shave, Nor let the hair grow long, — They shall only poll, their heads.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
And wine, shall no priest drink, —when they enter into the inner court.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
Neither widow nor divorced woman, shall they take to them to wife, — But, virgins of the seed of the house of Israel, Or a widow who shall be the widow of a priest shall they take.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
And my people, shall they instruct, between the holy and the common, — And between the unclean and the clean, shall they cause them to distinguish.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
And in a controversy, They shall stand up for justice, With my judgments, shall they judge it, And my laws and my statutes in all mine appointed assemblies, shall they observe, And my sabbaths, shall they hallow.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
And unto no dead person, shall they go in. to defile themselves, - Save that for father or for mother or for son or for daughter, for brother or for sister who hath belonged to no husband they may defile themselves.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
Yet after he is cleansed, seven days shall they count to him.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And in the day when he entereth into the sanctuary, into the inner court to minister in the sanctuary, He shall bring near his sin-bearer, Declareth My Lord Yahweh.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
So shall it become to them an inheritance, I, am their inheritance, - And possession, shall ye not give them in Israel, I am their possession.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
As for the meal-offering and the sin-bearer and the guilt-bearer, they shall eat them, —And everything devoted in Israel to them, shall belong.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
And the first of all the firstfruits of everything, and every heave-offering of everything, from among all your heave-offerings to the priests, shall it belong, — The first of your meal, shall ye give to the priest, To cause a blessing to rest upon by house.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
Nothing that died of itself or was torn in pieces, of bird or of beast shall be eaten by the priests.

< Ezekieli 44 >