< Ezekieli 34 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord came to me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
“Son of man, prophesy about the shepherds of Israel. Prophesy, and you shall say to the shepherds: Thus says the Lord God: Woe to the shepherds of Israel who feed themselves! Should not the flocks be fed by the shepherds?
3 Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
You consumed the milk, and you covered yourselves with the wool, and you killed what was fattened. But my flock you did not feed.
4 Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
What was weak, you have not strengthened, and what was sick, you have not healed. What was broken, you have not bound, and what was cast aside, you have not led back again, and what was lost, you have not sought. Instead, you ruled over them with severity and with power.
5 Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
And my sheep were scattered, because there was no shepherd. And they became devoured by all the wild beasts of the field, and they were dispersed.
6 Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
My sheep have wandered to every mountain and to every exalted hill. And my flocks have been scattered across the face of the earth. And there was no one who sought them; there was no one, I say, who sought them.
7 “‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
Because of this, O shepherds, listen to the word of the Lord:
8 Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
As I live, says the Lord God, since my flocks have become a prey, and my sheep have been devoured by all the wild beasts of the field, since there was no shepherd, for my shepherds did not seek my flock, but instead the shepherds fed themselves, and they did not feed my flocks:
9 Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
because of this, O shepherds, listen to the word of the Lord:
10 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
Thus says the Lord God: Behold, I myself will be over the shepherds. I will require my flock at their hand, and I will cause them to cease, so that they no longer refrain from feeding the flock. Neither will the shepherds feed themselves any more. And I will deliver my flock from their mouth; and it will no longer be food for them.
11 “‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
For thus says the Lord God: Behold, I myself will seek my sheep, and I myself will visit them.
12 Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
Just as a shepherd visits his flock, in the day when he will be in the midst of his sheep that were scattered, so will I visit my sheep. And I will deliver them from all the places to which they had been scattered in the day of gloom and darkness.
13 Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
And I will lead them away from the peoples, and I will gather them from the lands, and I will bring them into their own land. And I will pasture them on the mountains of Israel, by the rivers, and in all the settlements of the land.
14 Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
I will feed them in very fertile pastures, and their pastures will be on the lofty mountains of Israel. There they will rest on the green grass, and they will be fed in the fat pastures, on the mountains of Israel.
15 Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I will feed my sheep, and I will cause them to lie down, says the Lord God.
16 Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
I will seek what had been lost. And I will lead back again what had been cast aside. And I will bind up what had been broken. And I will strengthen what had been infirm. And I will preserve what was fat and strong. And I will feed them on judgment.
17 “‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
But as for you, O my flocks, thus says the Lord God: Behold, I judge between cattle and cattle, among rams and among he-goats.
18 Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
Was it not enough for you to feed upon good pastures? For you even trample with your feet upon the remainder of your pastures. And when you drank the purist water, you disturbed the remainder with your feet.
19 Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
And my sheep were pastured from what you had trampled with your feet, and they drank from what your feet had disturbed.
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
Because of this, thus says the Lord God to you: Behold, I myself am judging between the fat cattle and the lean.
21 Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
For you have pushed with your sides and shoulders, and you have threatened all the weak cattle with your horns, until they were scattered abroad.
22 tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
I will save my flock, and it will no longer be a prey, and I will judge between cattle and cattle.
23 Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
And I will raise up over them ONE SHEPHERD, who will feed them, my servant David. He himself will feed them, and he will be their shepherd.
24 Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
And I, the Lord, will be their God. And my servant David will be the leader in their midst. I, the Lord, have spoken.
25 “‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
And I will make a covenant of peace with them. And I will cause the very harmful beasts to cease from the land. And those who are living in the desert will sleep securely in the forests.
26 Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
And I will make them a blessing all around my hill. And I will send the rain in due time; there will be showers of blessing.
27 Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
And the tree of the field will yield its fruit, and the land will yield its crop. And they will be in their own land without fear. And they shall know that I am the Lord, when I will have crushed the chains of their yoke, and when I will have rescued them from the hand of those who rule over them.
28 Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
And they will no longer be a prey to the Gentiles, nor will the wild beasts of the earth devour them. Instead, they will live in confidence without any terror.
29 Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
And I will raise up for them a renowned branch. And they will be no longer be diminished by famine in the land, nor will they carry any longer the reproach of the Gentiles.
30 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And they shall know that I, the Lord their God, am with them, and that they are my people, the house of Israel, says the Lord God.
31 Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”
For you are my flocks; the flocks of my pasture are men. And I am the Lord your God, says the Lord God.”

< Ezekieli 34 >