< Ezekieli 27 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
and he seide, Therfor thou, sone of man, take weilyng on Tire.
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
And thou schalt seie to Tire, that dwellith in the entryng of the see, to the marchaundie of puplis to many ilis, The Lord God seith these thingis, O! Tire, thou seidist, Y am of perfit fairnesse,
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
and Y am set in the herte of the see. Thei that ben in thi coostis that bildiden thee, filliden thi fairnesse;
5 Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
thei bildiden thee with fir trees of Sanyr, with alle werkis of boordis of the see; thei token a cedre of the Liban, to make a mast to thee.
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
Thei hewiden ookis of Bala in to thin ooris, thei maden to thee thi seetis of roweris of yuer of Ynde, and cabans of the ilis of Italie.
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
Dyuerse biys, `ether whijt silk, of Egipt, was wouun to thee in to a veil, that it schulde be set in the mast; iacynct and purpur of the ilis of Elisa weren maad thin hiling.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
The dwelleris of Sidon and Aradians weren thi roweris; Tire, thi wise men weren maad thi gouernouris.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
The elde men of Biblos, and the prudent men therof, hadden schipmen to the seruyse of thi dyuerse araye of houshold; alle the schippis of the see, and the schip men of tho, weren in the puple of thi marchaundie.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
Perseis, and Lidians, and Libians weren in thin oost; thi men werriours hangiden in thee a scheeld and helm, for thin ournyng.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
Sones Aradians with thin oost weren on thi wallis in thi cumpas; but also Pigmeis, that weren in thi touris, hangiden her arowe casis in thi wallis bi cumpas; thei filliden thi fairnesse.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Cartagynensis, thi marchauntis, of the multitude of alle richessis filliden thi feiris, with siluer, and irun, with tyn, and leed.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Greece, and Tubal, and Mosoch, thei weren thi marchauntis, and brouyten boonde men and brasun vessels to thi puple.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Fro the hous of Thogorma thei brouyten horsis, and horse men, and mulis, to thi chepyng.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
The sones of Dedan weren thi marchauntis; many ilis the marchaundie of thin hond, chaungiden teeth of yuer, and of hebennus, in thi prijs.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
Sirie was thi marchaunt, for the multitude of thi werkis thei settiden forth in thi marcat gemme, and purpur, and clothis wouun dyuersli at the maner of scheeldis, and bijs, and seelk, and cochod, ether auer de peis.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
Juda and the lond of Israel weren thi marchauntis in the beste wheete, and settiden forth in thi feiris bawme, and hony, and oile, and resyn.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
Damassen was thi marchaunt, in the multitude of thi werkis, in the multitude of dyuerse richessis, in fat wyn, in wollis of best colour.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
Dan, and Greece, and Mosel, settiden forth in thi fairis irun maad suteli, gumme of myrre, and calamus, that is, a spice swete smellynge, in thi marchaundie.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
Dedan weren thi marchauntis, in tapitis to sitte.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Arabie and alle the princes of Cedar, thei weren the marchauntis of thin hond; with lambren, and wetheris, and kidis thi marchauntis camen to thee.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
The silleris of Saba and of Rema, thei weren thi marchauntis, with alle the beste swete smellynge spices, and preciouse stoon, and gold, which thei settiden forth in thi marcat.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
Aran, and Chenne, and Eden, weren thi marchauntis; Sabba, and Assur, and Chelmath, weren thi silleris.
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
Thei weren thi marchaundis in many maneres, in fardels of iacinct and of clothis of many colours, and of preciouse richessis, that weren wlappid and boundun with coordis.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
Also schippis of the see hadden cedris in her marchaundies; thi princes weren in thi marchaundie; and thou were fillid, and were glorified greetli in the herte of the see.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
Thi rowers brouyten thee in many watris, the south wynd al to-brak thee; in the herte of the see weren thi richessis,
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
and thi tresours, and thi many fold instrument. Thi schip men, and thi gouernouris that helden thi purtenaunce of houshold, and weren souereyns of thi puple, and thi men werriours that weren in thee, with al thi multitude which is in the myddis of thee, schulen falle doun in the herte of the see, in the dai of thi fallyng.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
Schippis schulen be disturblid of the sown of the cry of thi gouernours;
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
and alle men that helden oore, schulen go doun of her shippis. Shipmen and alle gouernouris of the see shulen stonde in the lond;
30 Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
and schulen yelle on thee with greet vois. And thei shulen cry bitterli, and thei schulen caste poudur on her heedis, and schulen be spreynt with aische.
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
And thei schulen shaue ballidnesse on thee, and schulen be gird with hairis, and thei schulen biwepe thee in bitternesse of soule, with most bittir wepyng.
32 Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
And thei schulen take on thee a song of mourenyng, and thei schulen biweile thee, Who is as Tire, that was doumb in the myddis of the see?
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
And thou, Tire, fillidist many puplis in the goyng out of thi marchaundies of the see; in the multitude of thi richessis, and of thi puplis, thou madist riche the kingis of erthe.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
Now thou art al to-brokun of the see, in the depthis of watris. Thi richessis and al thi multitude that was in the myddis of thee fellen doun;
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
alle the dwelleris of ilis and the kyngis of tho weren astonyed on thee. Alle thei weren smytun with tempest, and chaungiden cheris;
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
the marchauntis of puplis hissiden on thee. Thou art brouyt to nouyt, and thou schalt not be til `in to with outen ende.

< Ezekieli 27 >