< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
And it was doon in the seuenthe yeer, in the fyuethe monethe, in the tenthe dai of the monethe, men of the eldris of Israel camen to axe the Lord; and thei saten bifor me.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord was maad to me,
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
and he seide, Sone of man, speke thou to the eldere men of Israel; and thou schalt seie to hem, The Lord God seith these thingis, Whether ye camen to axe me? Y lyue, for Y schal not answere to you, seith the Lord God. Sone of man,
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
if thou demest hem, if thou demest, schewe thou to hem the abhomynaciouns of her fadris.
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
And thou schalt seie to hem, The Lord God seith these thingis, In the dai in which Y chees Israel, and reiside myn hond for the generacioun of the hous of Jacob, and Y apperide to hem in the lond of Egipt, and Y reiside myn hond for hem, and Y seide, Y am youre Lord God,
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
in that dai Y reiside myn hond for hem, that Y schulde leede hem out of the lond of Egipt, in to the lond which Y hadde purueiede to hem, the lond flowynge with mylk and hony, which is noble among alle londis.
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
And Y seide to hem, Ech man caste awei the offenciouns of hise iyen, and nyle ye be defoulid in the idols of Egipt; Y am youre Lord God.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
And thei terriden me to wraththe, and nolden here me; ech man castide not awei the abhomynaciouns of hise iyen, nether thei forsoken the idols of Egipt.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
And Y seide, that Y wold schede out myn indignacioun on hem, and fille my wraththe in hem, in the myddis of the lond of Egipt. And Y dide for my name, that it schulde not be defoulid bifore hethene men, in the myddis of whiche thei weren, and among whiche Y apperide to hem, that Y schulde lede hem out of the lond of Egipt.
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
Therfor Y castide hem out of the lond of Egipt, and Y ledde hem out in to desert;
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
and Y yaf to hem my comaundementis, and Y schewide to hem my doomes, which a man schal do, and lyue in tho.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
Ferthermore and Y yaf to hem my sabatis, that it schulde be a sygne bitwixe me and hem, and that thei schulden wite, that Y am the Lord halewynge hem.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
And the hous of Israel terriden me to wraththe in desert; thei yeden not in my comaundementis, and thei castiden awei my domes, whiche a man that doith, schal lyue in tho; and thei defouliden greetli my sabatis. Therfor Y seide, that Y wolde schede out my strong veniaunce on hem in desert, and waste hem;
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
and Y dide for my name, lest it were defoulid bifor hethene men, fro whiche Y castide hem out in the siyt of tho.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
Therfor Y reiside myn hond on hem in the desert, that Y brouyte not hem in to the lond which Y yaf to hem, the lond flowynge with mylk and hony, the beste of alle londis.
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
For thei castiden awei my domes, and yeden not in my comaundementis, and thei defouliden my sabatis; for the herte of hem yede after idols.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
And myn iye sparide on hem, that Y killide not hem, nether Y wastide hem in the desert.
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
Forsothe Y seide to the sones of hem in wildirnesse, Nyle ye go in the comaundementis of youre fadris, nether kepe ye the domes of hem, nethir be ye defoulid in the idols of hem.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
Y am youre Lord God, go ye in my comaundementis, and kepe ye my domes, and do ye tho.
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
And halowe ye my sabatis, that it be a signe bitwixe me and you, and that it be knowun, that Y am youre Lord God.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
And the sones terriden me to wraththe, and yeden not in my comaundementis, and kepten not my domes, that thei diden tho, whiche whanne a man hath do, he schal lyue in tho, and thei defouliden my sabatis. And Y manaasside to hem, that Y wolde schede out my stronge veniaunce on hem, and fille my wraththe in hem in the desert.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
But Y turnede awei myn hond, and Y dide this for my name, that it were not defoulid bifore hethene men, fro whiche Y castide hem out bifore the iyen of tho.
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
Eft Y reiside myn hond ayens hem in wildirnesse, that Y schulde scatere hem in to naciouns, and wyndewe hem in to londis;
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
for that that thei hadden not do my domes, and hadden repreuyd my comaundementis, and hadden defoulid my sabatis, and her iyen hadden be after the idols of her fadris.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Therfor and Y yaf to hem comaundementis not good, and domes in whiche thei schulen not lyue.
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
And Y defoulide hem in her yiftis, whanne thei offriden to me for her trespassis al thing that openeth the wombe; and thei schulen wite, that Y am the Lord.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Wherfor speke thou, sone of man, to the hous of Israel, and thou schalt seie to hem, The Lord God seith these thingis, Yit and in this youre fadris blasfemyden me, whanne thei dispisynge hadden forsake me,
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
and Y hadde brouyte hem in to the lond on which Y reiside myn hond, that Y schulde yiue to hem, thei siyen ech hiy litil hil, and ech tree ful of boowis, and thei offriden there her sacrifices, and thei yauen there her offryngis, in to terring to wraththe; and thei settiden there the odour of her swetnesse, and thei offriden her moiste sacrifices.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
And Y seide to hem, What is the hiy thing, to whiche ye entren? And the name therof is clepid Hiy Thing til to this dai.
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Therfor seie thou to the hous of Israel, The Lord God seith these thingis, Certis ye ben defoulid in the weie of youre fadris, and ye don fornycacioun aftir the offendingis of hem,
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
and in the offryng of youre yiftis, whanne ye leden ouer youre sones bi fier, ye ben defoulid in alle youre idols til to dai, and schal Y answere to you, the hous of Israel? Y lyue, seith the Lord God, for Y schal not answere to you;
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
nether the thouyte of youre soul schal be don, that seien, We schulen be as hethene men, and as naciouns of erthe, that we worschipe trees and stoonys.
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Y lyue, seith the Lord God, for in strong hond, and in arm stretchid forth, and in strong veniaunce sched out, I schal regne on you.
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
And Y schal lede out you fro puplis, and Y schal gadere you fro londis, in whiche ye ben scaterid; in strong hond, and in arm stretchid forth, and in strong veniaunce sched out Y schal regne on you.
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
And Y schal bringe you in to desert of puplis, and Y schal be demed there with you face to face.
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
As Y stryuede in doom ayens youre fadris in the desert of the lond of Egipt, so Y schal deme you, seith the Lord;
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
and Y schal make you suget to my septre, and Y schal bringe in you in the boondis of pees.
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And Y schal chese of you trespassouris, and wickid men; and Y schal leede hem out of the lond of her dwelling, and thei schulen not entre in to the lond of Israel; and ye schulen wite, that Y am the Lord.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
And ye, the hous of Israel, the Lord God seith these thingis, Go ye ech man aftir youre idols, and serue ye tho. That and if ye heren not me in this, and defoulen more myn hooli name in youre yiftis,
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
and in youre idols, in myn hooli hil, in the hiy hil of Israel, seith the Lord God, ye schulen be punyschid greuousliere. There al the hous of Israel schal serue me, sotheli alle men in the lond, in which thei schulen plese me; and there Y schal seke youre firste fruytis, and the bigynnyng of youre tithis in alle youre halewyngis.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Y schal resseiue you in to odour of swetnesse, whanne Y schal leede you out of puplis, and schal gadere you fro londis, in whiche ye weren scaterid; and Y schal be halewid in you bifor the iyen of naciouns.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
And ye schulen wite, that Y am the Lord, whanne Y schal bringe you in to the lond of Israel, in to the lond for which Y reiside myn hond, that Y schulde yyue it to youre fadris.
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
And ye schulen haue mynde there on youre weies, and on alle youre grete trespassis, bi whiche ye ben defoulid in tho; and ye schulen displese you in youre siyt, in alle youre malices whiche ye diden.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
And ye schulen wite, that Y am the Lord, whanne Y schal do wel to you for my name; not bi youre yuel weies, nether bi youre worste trespassis, ye hous of Israel, seith the Lord God.
45 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord was maad to me,
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
and he seide, Thou, sone of man, sette thi face ayens the weie of the south, and droppe thou to the south, and profesie thou to the forest of the myddai feeld.
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
And thou schalt seie to the myddai forest, Here thou the word of the Lord. The Lord God seith these thingis, Lo! Y schal kyndle a fier in thee, and Y schal brenne in thee ech green tre, and ech drie tre; the flawme of brennyng schal not be quenchid, and ech face schal be brent ther ynne, fro the south til to the north.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
And ech man schal se, that Y the Lord haue kyndlid it, and it schal not be quenchid.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
And Y seide, A! A! A! Lord God, thei seien of me, Whethir this man spekith not bi parablis?

< Ezekieli 20 >