< Ezekieli 25 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
and he seide, Thou, sone of man, sette thi face ayens the sones of Amon, and thou schalt profesie of hem.
3 Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
And thou schalt seie to the sones of Amon, Here ye the word of the Lord God; the Lord God seith these thingis, For that that ye seiden, Wel! wel! on my seyntuarie, for it is defoulid, and on the lond of Israel, for it is maad desolat, and on the hous of Juda, for thei ben led in to to caitifte; lo!
4 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
therfor Y schal yyue thee the sones of the eest in to eritage, and thei schulen sette her foldis in thee, and thei shulen sette her tentis in thee; thei schulen ete thi fruytis, and thei schulen drynke thi mylk.
5 Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And Y schal yyue Rabath in to a dwellyng place of camels, and the sones of Amon in to a bed of beestis; and ye schulen wite, that Y am the Lord.
6 Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
For the Lord God seith these thingis, For that that thou flappidist with hond, and smytidist with the foot, and ioyedist of al desijr on the lond of Israel;
7 Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
therfor lo! Y schal stretche forth myn hond on thee, and Y schal yyue thee in to rauyschyng of hethene men, and Y schal sle thee fro puplis, and Y schal leese thee, and al to-breke thee fro londis; and ye schulen wite, that Y am the Lord.
8 “Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
The Lord God seith these thingis, For that that Moab and Seir seiden, Lo! the hous of Juda is as alle folkis; therfor lo!
9 Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
Y schal opene the schuldre of Moab of citees, sotheli of citees therof and of the endis therof, the noble citees of the lond, Bethiesmoth, and Beelmoth,
10 Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
and Cariathaym, to the sones of the eest, with the sones of Amon. And Y schal yyue it in to eritage, that mynde of the sones of Amon be no more among hethene men,
11 Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
and in Moab Y schal make domes; and thei schulen wite, that Y am the Lord.
12 “Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
The Lord God seith these thingis, For that that Ydumee dide veniaunce, that it avengide it silf of the sones of Juda, and synnede doynge trespas, and axide greetli veniaunce of hem;
13 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
therfor the Lord God seith these thingis, Y schal stretche forth myn hond on Idumee, and Y schal take awei fro it man and beeste, and Y schal make it desert of the south; and thei that ben in Dedan schulen falle bi swerd.
14 Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
And Y schal yyue my veniaunce on Idumee, bi the hond of my puple Israel; and thei schulen do in Edom bi my wraththe, and bi my strong veniaunce; and thei schulen knowe my veniaunce, seith the Lord God.
15 “Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
The Lord God seith these thingis, For that that Palestyns diden veniaunce, and auengiden hem silf, with al wille sleynge, and fillynge elde enemytees;
16 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
therfor the Lord God seith these thingis, Lo! Y schal stretche forth myn hond on Palestyns, and Y schal sle sleeris, and Y schal leese the remenauntis of the se coost;
17 Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
and Y schal make grete veniaunces in hem, and Y schal repreue in strong veniaunce; and thei schulen wite, that Y am the Lord, whanne Y schal yyue my veniaunce on hem.

< Ezekieli 25 >