< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
Dlaczego powtarzacie między sobą takie przysłowie o ziemi Izraela, mówiąc: Ojcowie jedli kwaśne winogrona, a synom zęby cierpną.
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
Jak żyję, mówi Pan BÓG, nie będziecie więcej powtarzać tego przysłowia w Izraelu.
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
Oto wszystkie dusze są moje, tak dusza ojca, jak i dusza syna jest moja. Dusza, która grzeszy, ona umrze.
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
Lecz jeśli człowiek jest sprawiedliwy i wykonuje sąd i sprawiedliwość;
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
I nie jadał na górach, nie podnosi swych oczu ku bożkom domu Izraela ani nie hańbił żony swego bliźniego, ani nie zbliżał się do kobiety podczas jej nieczystości;
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
Nikogo nie uciskał, zwracał zastaw dłużnikowi, nie popełnił grabieży, dawał swój chleb głodnemu i przyodziewał nagiego szatą;
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
Nie uprawiał lichwy i nie brał odsetek, odwracał swą rękę od nieprawości i sprawiedliwy sąd wykonywał między jednym człowiekiem a drugim;
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
Postępował według moich ustaw i przestrzegał moich sądów, czyniąc to, co prawe – ten jest sprawiedliwy, na pewno żyć będzie, mówi Pan BÓG.
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
A [jeśli] spłodził syna zbójcę i rozlewającego krew, który popełnił jedną z tych rzeczy;
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
Który żadnej z tamtych dobrych rzeczy nie czynił, ale raczej jadał na górach, hańbił żonę swego bliźniego;
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
Uciskał ubogiego i nędznego, popełniał grabież, nie zwracał zastawu, podnosił oczy ku bożkom, czynił obrzydliwość;
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
Uprawiał lichwę i brał odsetki – czy ten będzie żył? Nie będzie żył, [ponieważ] popełnił te wszystkie obrzydliwości. Ten na pewno umrze. Jego krew spadnie na niego.
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
A oto jeśli spłodził syna, który widział wszystkie grzechy swego ojca, jakie czynił, a widząc [je], nie czynił nic podobnego;
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
Nie jadał na górach, nie podnosił swych oczu ku bożkom domu Izraela, nie hańbił żony swego bliźniego;
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
Nikogo nie uciskał, nie zatrzymywał zastawu, nie popełniał grabieży, dawał swój chleb głodnemu i przyodziewał szatą nagiego;
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
Odwracał swą rękę [od ucisku] nad ubogim, nie uprawiał lichwy i nie brał odsetek, wykonywał moje sądy i postępował według moich ustaw – ten nie umrze za nieprawość swego ojca, ale na pewno będzie żył.
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
[Lecz] jego ojciec, ponieważ czynił krzywdę, popełniał grabież i nie czynił tego, co dobre pośród swego ludu, oto umrze za swoją nieprawość.
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
Ale mówicie: Czemu? Czy syn nie ponosi [kary] za nieprawość ojca? Gdy syn czynił to, co prawe i sprawiedliwe, i przestrzegał wszystkich moich ustaw, i wypełniał je, na pewno będzie żył.
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
Dusza, która grzeszy, umrze. Syn nie poniesie kary za nieprawość ojca ani ojciec nie poniesie kary za nieprawość syna. Sprawiedliwość sprawiedliwego pozostanie na nim, a niegodziwość niegodziwego pozostanie na nim.
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
A jeśli niegodziwy odwróci się od wszystkich swoich grzechów, które popełnił, będzie strzegł wszystkich moich ustaw i będzie czynił to, co prawe i sprawiedliwe, na pewno będzie żył, nie umrze;
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
Żadne jego występki, których się dopuścił, nie będą mu wspominane. Będzie żył w swej sprawiedliwości, którą czynił.
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
Czyż ja mam upodobanie w śmierci niegodziwego? – mówi Pan BÓG, a nie raczej w tym, aby się odwrócił od swoich dróg i żył?
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
Ale [jeśli] sprawiedliwy odwróci się od swojej sprawiedliwości i popełni nieprawość, czyniąc według wszystkich obrzydliwości, które popełnia niegodziwy, czy taki będzie żył? Wszystkie jego sprawiedliwości, które czynił, nie będą wspominane. Z powodu swego przestępstwa, które popełniał, i z powodu swego grzechu, którego się dopuścił, z powodu tych [rzeczy] umrze.
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
Ale mówicie: Droga PANA nie jest słuszna. Słuchajcie teraz, domu Izraela: Czy moja droga nie jest prosta? Czy raczej wasze drogi są niesłuszne?
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
Gdy sprawiedliwy odwróci się od swojej sprawiedliwości, a czyniąc nieprawość umrze, to z powodu swojej nieprawości, którą czynił, umrze.
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
Ale gdy niegodziwy odwróci się od swojej niegodziwości, której się dopuścił, a czyni to, co prawe i sprawiedliwe, ten zachowa swoją duszę.
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
Ponieważ zastanowił się i odwrócił się od wszystkich swoich występków, których się dopuścił, na pewno będzie żył, nie umrze.
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
[A jednak] dom Izraela mówi: Droga PANA nie jest słuszna. Czy moje drogi nie są słuszne, domu Izraela? Czy [raczej] wasze drogi [są] niesłuszne?
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
Dlatego, domu Izraela, będę sądzić każdego z was według jego dróg, mówi Pan BÓG. Nawróćcie się i odwróćcie się od wszystkich swoich występków, aby nieprawość nie stała się waszą zgubą.
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
Odrzućcie od siebie wszystkie swoje przestępstwa, których się dopuszczaliście, i uczyńcie sobie nowe serce i nowego ducha. Czemu macie umrzeć, domu Izraela?
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
Nie mam bowiem żadnego upodobania w śmierci umierającego, mówi Pan BÓG. Odwróćcie się więc, a będziecie żyć.

< Ezekieli 18 >