< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
و کلام خداوند بر من نازل شده، گفت:۱
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
«شما چه‌کار دارید که این مثل رادرباره زمین اسرائیل می‌زنید و می‌گویید: پدران انگور ترش خوردند و دندانهای پسران کندگردید.»۲
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
خداوند یهوه می‌گوید: «به حیات خودم قسم که بعد از این این مثل را در اسرائیل نخواهیدآورد.۳
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
اینک همه جانها از آن منند چنانکه جان پدر است، همچنین جان پسر نیز، هردوی آنها ازآن من می‌باشند. هر کسی‌که گناه ورزد او خواهدمرد.۴
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
و اگر کسی عادل باشد و انصاف و عدالت رابعمل آورد،۵
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
و بر کوهها نخورد و چشمان خودرا بسوی بتهای خاندان اسرائیل برنیفرازد و زن همسایه خود را بی‌عصمت نکند و به زن حایض نزدیکی ننماید،۶
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
و بر کسی ظلم نکند و گروقرضدار را به او رد نماید و مال کسی را به غصب نبرد، بلکه نان خود را به گرسنگان بدهد وبرهنگان را به‌جامه بپوشاند،۷
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
و نقد را به سودندهد و ربح نگیرد، بلکه دست خود را از ستم برداشته، انصاف حقیقی را در میان مردمان اجرادارد،۸
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
و به فرایض من سلوک نموده و احکام مرانگاه داشته، به راستی عمل نماید. خداوند یهوه می‌فرماید که آن شخص عادل است و البته زنده خواهد ماند.۹
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
«اما اگر او پسری ستم پیشه و خونریز تولیدنماید که یکی از این کارها را بعمل آورد،۱۰
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
وهیچکدام از آن اعمال نیکو را بعمل نیاورد بلکه برکوهها نیز بخورد و زن همسایه خود را بی‌عصمت سازد،۱۱
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
و بر فقیران و مسکینان ظلم نموده، مال مردم را به غصب ببرد و گرو را پس ندهد، بلکه چشمان خود را بسوی بتها برافراشته، مرتکب رجاسات بشود،۱۲
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
و نقد را به سود داده، ربح گیرد، آیا او زنده خواهد ماند؟ البته او زنده نخواهد ماند و به‌سبب همه رجاساتی که بجاآورده است خواهد مرد و خونش بر سرش خواهد بود.۱۳
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
«و اگر پسری تولید نماید که تمامی گناهان را که پدرش بجا می‌آورد دیده، بترسد و مثل آنهاعمل ننماید،۱۴
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
و بر کوهها نخورد و چشمان خود را بسوی بتهای خاندان اسرائیل برنیفرازد وزن همسایه خویش را بی‌عصمت نکند،۱۵
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
و برکسی ظلم نکند و گرو نگیرد و مال احدی را به غصب نبرد بلکه نان خود را به گرسنگان دهد وبرهنگان را به‌جامه پوشاند،۱۶
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
و دست خود را ازفقیران برداشته، سود و ربح نگیرد و احکام مرا بجاآورده، به فرایض من سلوک نماید، او به‌سبب گناه پدرش نخواهد مرد بلکه البته زنده خواهد ماند.۱۷
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
و اما پدرش چونکه با برادران خود به شدت ظلم نموده، مال ایشان را غصب نمود و اعمال شنیع را در میان قوم خود بعمل آورد او البته به‌سبب گناهانش خواهد مرد.۱۸
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
«لیکن شما می‌گویید چرا چنین است؟ آیاپسر متحمل گناه پدرش نمی باشد؟ اگر پسرانصاف و عدالت را بجا آورده، تمامی فرایض مرانگاه دارد و به آنها عمل نماید، او البته زنده خواهد ماند.۱۹
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
هر‌که گناه کند او خواهد مرد. پسر متحمل گناه پدرش نخواهد بود و پدرمتحمل گناه پسرش نخواهد بود. عدالت مردعادل بر خودش خواهد بود و شرارت مرد شریربر خودش خواهد بود.۲۰
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
«و اگر مرد شریر از همه گناهانی که ورزیده باشد بازگشت نماید و جمیع فرایض مرا نگاه داشته، انصاف و عدالت را بجا آورد او البته زنده مانده نخواهد مرد.۲۱
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
تمامی تقصیرهایی که کرده باشد به ضد او به یاد آورده نخواهد شد بلکه در عدالتی که کرده باشد زنده خواهد ماند.»۲۲
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
خداوند یهوه می‌فرماید: «آیا من از مردن مرد شریر مسرور می‌باشم؟ نی بلکه از اینکه ازرفتار خود بازگشت نموده، زنده ماند.۲۳
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
و اگرمرد عادل از عدالتش برگردد و ظلم نموده، موافق همه رجاساتی که شریران می‌کنند عمل نماید آیااو زنده خواهد ماند؟ نی بلکه تمامی عدالت او که کرده است به یاد آورده نخواهد شد و در خیانتی که نموده و در گناهی که ورزیده است خواهدمرد.۲۴
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
«اما شما می‌گویید که طریق خداوندموزون نیست. پس حال‌ای خاندان اسرائیل بشنوید: آیا طریق من غیر موزون است و آیاطریق شما غیر موزون نیست؟۲۵
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
چونکه مردعادل از عدالتش برگردد و ظلم کند در آن خواهدمرد. به‌سبب ظلمی که کرده است خواهد مرد.۲۶
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
و چون مرد شریر را از شرارتی که کرده است بازگشت نماید و انصاف و عدالت را بجا آورد، جان خود را زنده نگاه خواهد داشت.۲۷
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
چونکه تعقل نموده، از تمامی تقصیرهایی که کرده بودبازگشت کرد البته زنده خواهد ماند و نخواهدمرد.۲۸
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
لیکن شما‌ای خاندان اسرائیل می‌گوییدکه طریق خداوند موزون نیست. ای خاندان اسرائیل آیا طریق من غیر موزون است و آیاطریق شما غیر موزون نیست؟»۲۹
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
بنابراین خداوند یهوه می‌گوید: «ای خاندان اسرائیل من برهریک از شما موافق رفتارش داوری خواهم نمود. پس توبه کنید و از همه تقصیرهای خودبازگشت نمایید تا گناه موجب هلاکت شما نشود.۳۰
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
تمامی تقصیرهای خویش را که مرتکب آنها شده‌اید از خود دور اندازید و دل تازه و روح تازه‌ای برای خود ایجاد کنید. زیرا که‌ای خاندان اسرائیل برای چه بمیرید؟۳۱
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
زیرا خداوند یهوه می‌گوید: من از مرگ آنکس که می‌میرد مسرورنمی باشم. پس بازگشت نموده، زنده مانید.»۳۲

< Ezekieli 18 >