< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l'Éternel me fut encore adressée en ces termes:
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
Que voulez-vous dire, vous qui répétez continuellement ce proverbe, dans le pays d'Israël, en disant: “Les pères ont mangé du raisin vert, et les dents des enfants en sont agacées?”
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
Je suis vivant! dit le Seigneur, l'Éternel, vous n'aurez plus lieu de répéter ce proverbe en Israël.
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
Voici, toutes les âmes sont à moi, l'âme du père comme l'âme du fils; toutes deux sont à moi; l'âme qui pèche est celle qui mourra.
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
L'homme qui est juste, qui pratique la droiture et la justice,
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
Qui ne mange point sur les montagnes, qui ne lève pas les yeux vers les idoles de la maison d'Israël, qui ne déshonore pas la femme de son prochain, ni ne s'approche d'une femme pendant sa souillure;
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
L'homme qui ne fait de tort à personne, qui rend au débiteur son gage, qui ne commet point de rapine, qui donne de son pain à l'affamé, et couvre d'un vêtement celui qui est nu,
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
Qui ne prête point à usure, qui ne retient pas au-delà de ce qui lui est dû, qui détourne sa main de l'iniquité, qui rend son jugement selon la vérité entre un homme et un autre,
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
Qui marche selon mes statuts et observe mes ordonnances, en se conduisant avec droiture, - cet homme est juste, et certainement il vivra, dit le Seigneur, l'Éternel.
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
Mais s'il a donné le jour à un fils violent, qui répande le sang, et ne fasse à son frère que l'une de ces choses et non pas les autres;
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
Qu'il mange sur les montagnes, qu'il déshonore la femme de son prochain,
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
Qu'il fasse tort à l'affligé et au pauvre, qu'il commette des rapines et ne rende point le gage, qu'il lève les yeux vers les idoles et commette des abominations,
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
Qu'il prête à usure, qu'il retienne plus qu'il ne lui est dû, - ce fils-là vivrait-il? Il ne vivra pas! Parce qu'il a commis toutes ces abominations, certainement il mourra, et son sang sera sur lui.
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
Mais voici, si ce dernier à son tour a donné le jour à un fils qui voie tous les péchés qu'a commis son père, et qui prenne soin de ne rien faire de semblable;
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
Qu'il ne mange point sur les montagnes, qu'il ne lève point les yeux vers les idoles de la maison d'Israël, qu'il ne déshonore pas la femme de son prochain,
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
Qu'il ne fasse tort à personne, qu'il ne retienne point le gage et ne commette point de rapine, qu'il donne de son pain à l'affamé, et couvre d'un vêtement celui qui est nu;
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
Qu'il détourne sa main de l'iniquité, qu'il ne retienne ni usure ni bénéfice, qu'il observe mes ordonnances et marche selon mes statuts, - cet homme ne mourra point pour l'iniquité de son père; certainement il vivra.
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
Mais c'est son père, qui a usé de violences et commis des rapines envers son frère, et fait ce qui n'est pas bien, au milieu de son peuple, voici, c'est lui qui mourra pour son iniquité.
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
Et vous dites: “Pourquoi le fils ne porte-t-il pas l'iniquité de son père? “C'est que le fils a agi selon la droiture et la justice, c'est qu'il a gardé tous mes statuts et les a mis en pratique; certainement il vivra.
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
L'âme qui pèche est celle qui mourra. Le fils ne portera point l'inquité du père, et le père ne portera point l'iniquité du fils; la justice du juste sera sur lui, et la méchanceté du méchant sera sur lui.
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
Si le méchant se détourne de tous les péchés qu'il a commis, s'il garde tous mes statuts, et s'il agit selon la droiture et la justice, certainement il vivra et ne mourra point.
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
On ne se souviendra contre lui d'aucune de toutes les transgressions qu'il aura commises; il vivra à cause de la justice qu'il aura pratiquée.
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
Prendrais-je plaisir en aucune manière à la mort du méchant? dit le Seigneur, l'Éternel; n'est-ce pas plutôt à ce qu'il se détourne de ses voies et qu'il vive?
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
Mais si le juste se détourne de sa justice, qu'il commette l'iniquité, en suivant toutes les abominations que le méchant a accoutumé de commettre, vivrait-il? On ne se souviendra plus d'aucun des actes de justice qu'il aura accomplis, à cause de l'infidélité dont il s'est rendu coupable, et du péché qu'il a commis; c'est à cause de cela qu'il mourra.
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
Et vous dites: “La voie du Seigneur n'est pas bien réglée. “Écoutez maintenant, maison d'Israël: Est-ce ma voie qui n'est pas bien réglée? Ne sont-ce pas plutôt vos voies qui ne sont pas bien réglées?
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
Si le juste se détourne de sa justice, qu'il commette l'iniquité, que pour cela il meure, c'est à cause de l'iniquité qu'il a commise qu'il meurt.
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
Et si le méchant se détourne de la méchanceté qu'il a commise, et qu'il pratique la droiture et la justice, il fera vivre son âme.
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
S'il ouvre les yeux, et se détourne de toutes les transgressions qu'il a commises, certainement il vivra et ne mourra point.
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
Cependant la maison d'Israël dit: “La voie du Seigneur n'est pas bien réglée. “Sont-ce mes voies, ô maison d'Israël, qui ne sont pas bien réglées? Ne sont-ce pas plutôt vos voies qui ne sont pas bien réglées?
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
C'est pourquoi je vous jugerai chacun selon ses voies, ô maison d'Israël, dit le Seigneur, l'Éternel. Convertissez-vous, et détournez-vous de toutes vos transgressions, afin que l'iniquité ne devienne point pour vous une cause de ruine.
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
Rejetez loin de vous toutes les transgressions dont vous vous êtes rendus coupables, et faites-vous un cœur nouveau et un esprit nouveau; car pourquoi mourriez-vous, ô maison d'Israël?
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
En effet, je ne prends point plaisir à la mort de celui qui meurt, dit le Seigneur l'Éternel; convertissez-vous et vivez!

< Ezekieli 18 >