< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l'Eternel me fut encore [adressée], en disant:
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
Que voulez-vous dire, vous qui usez ordinairement de ce proverbe touchant le pays d'Israël, en disant: les pères ont mangé le verjus et les dents des enfants en sont agacées?
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
Je [suis] vivant, dit le Seigneur l'Eternel, que vous n'userez plus de ce proverbe en Israël.
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
Voici, toutes les âmes sont à moi; l'âme de l'enfant est à moi comme l'âme du père; [et] l'âme qui péchera [sera] celle [qui] mourra.
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
Mais l'homme qui sera juste, et qui fera ce qui est juste et droit;
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
Qui n'aura point mangé sur les montagnes, et qui n'aura point levé ses yeux vers les idoles de la maison d'Israël, et n'aura point souillé la femme de son prochain, et ne se sera point approché de la femme dans son état d'impureté,
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
Et qui n'aura foulé personne, qui aura rendu le gage à son débiteur, qui n'aura point ravi le bien d'autrui, qui aura donné de son pain à celui qui avait faim, et qui aura couvert d'un vêtement celui qui était nu;
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
Qui n'aura point prêté à usure, et n'aura point pris de surcroît; qui aura détourné sa main de l'iniquité; qui aura rendu un droit jugement entre les parties qui plaident ensemble,
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
Qui aura marché dans mes statuts, et aura gardé mes ordonnances pour agir en vérité, celui-là est juste; certainement il vivra, dit le Seigneur l'Eternel.
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
Que s'il a engendré un enfant qui soit un meurtrier, répandant le sang, et commettant des choses semblables;
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
Et qui ne fasse aucune de ces choses, [que j'ai commandées], mais qu'il mange sur les montagnes, qu'il corrompe la femme de son prochain,
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
Qu'il foule l'affligé, et le pauvre, qu'il ravisse le bien d'autrui, et qu'il ne rende point le gage, qu'il lève ses yeux vers les idoles et commette des abominations;
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
Qu'il donne à usure, et qu'il prenne du surcroît: vivra-t-il? Il ne vivra pas, quand il aura commis toutes ces abominations, on le fera mourir de mort, et son sang sera sur lui.
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
Mais s'il engendre un fils qui voyant tous les péchés que son père aura commis, y prenne garde, et ne fasse pas de semblables choses;
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
Qu'il ne mange point sur les montagnes, et qu'il ne lève point ses yeux vers les idoles de la maison d'Israël, qu'il ne corrompe point la femme de son prochain;
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
Et qu'il ne foule personne; qu'il ne prenne point de gages; qu'il ne ravisse point le bien d'autrui, qu'il donne de son pain à celui qui a faim, et qu'il couvre celui qui est nu;
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
Qu'il retire sa main de dessus l'affligé, qu'il ne prenne ni usure ni surcroît, qu'il garde mes ordonnances, et qu'il marche dans mes statuts; il ne mourra point pour l'iniquité de son père, mais certainement il vivra.
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
Mais son père, parce qu'il a usé de fraude, et qu'il a ravi ce qui était à son frère, et fait parmi son peuple ce qui n'est pas bon, voici, il mourra pour son iniquité.
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
Mais, direz-vous: pourquoi un tel fils ne portera-t-il pas l'iniquité de son père? Parce qu'un tel fils a fait ce qui était juste et droit, et qu'il a gardé tous mes statuts, et les a faits; certainement il vivra.
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
L'âme qui péchera sera celle qui mourra. Le fils ne portera point l'iniquité du père, et le père ne portera point l'iniquité du fils; la justice du juste sera sur le [juste]; et la méchanceté du méchant sera sur le [méchant].
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
Que si le méchant se détourne de tous ses péchés qu'il aura commis, et qu'il garde tous mes statuts, et fasse ce qui est juste et droit, certainement il vivra, il ne mourra point.
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
Il ne lui sera point fait mention de tous ses crimes qu'il aura commis, [mais] il vivra pour sa justice, à laquelle il se sera adonné.
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
Prendrais-je en aucune manière plaisir à la mort du méchant, dit le Seigneur l'Eternel, et non plutôt qu'il se détourne de son train, et qu'il vive?
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
Mais si le juste se détourne de sa justice, et qu'il commette l'iniquité, selon toutes les abominations que le méchant a accoutumé de commettre, vivra-t-il? il ne sera point fait mention de toutes ses justices qu'il aura faites, à cause de son crime qu'il aura commis, et à cause de son péché qu'il aura fait; il mourra pour ces choses-là.
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
Et vous, vous dites: la voie du Seigneur n'est pas bien réglée. Ecoutez maintenant maison d'Israël; ma voie n'est-elle pas bien réglée? ne sont-ce pas plutôt vos voies qui ne sont pas bien réglées?
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
Quand le juste se détournera de sa justice, et qu'il commettra l'iniquité, il mourra pour ces choses-là; il mourra pour son iniquité qu'il aura commise.
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
Et quand le méchant se détournera de sa méchanceté qu'il aura commise, et qu'il fera ce qui est juste et droit, il fera vivre son âme.
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
Ayant donc considéré [sa conduite], et s'étant détourné de tous ses crimes qu'il aura commis, certainement il vivra, il ne mourra point.
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
Et la maison d'Israël dira: la voie du Seigneur l'Eternel n'est pas bien réglée. Ô maison d'Israël! mes voies ne sont-elles pas bien réglées? ne sont-ce pas plutôt vos voies qui ne sont pas bien réglées?
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
C'est pourquoi je jugerai un chacun de vous selon ses voies, ô maison d'Israël! dit le Seigneur. Convertissez-vous, et détournez-vous de tous vos péchés, et l'iniquité ne vous sera point en ruine.
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
Jetez loin de vous tous les crimes par lesquels vous avez péché; et faites-vous un nouveau cœur, et un esprit nouveau, et pourquoi mourriez-vous, ô maison d'Israël?
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
Car je ne prends point de plaisir à la mort de celui qui meurt, dit le Seigneur l'Eternel. Convertissez-vous donc, et vivez.

< Ezekieli 18 >