< Ezekieli 16 >
1 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of Yahweh came unto me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
Son of man Let Jerusalem know her abominations,
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
Therefore shalt thou say— Thus saith My Lord. Yahweh To Jerusalem, Thine origin and thy birth, were of the land of the Canaanite, — Thy father was the Amorite And thy mother a Hittite
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
And, as for thy birth, in the day thou wast born, Thy navel-cord was not cut, And, in water, wast thou not bathed to cleanse thee, — And, as for being salted, thou was not salted, And, as for being bandaged, thou wast not bandaged.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
No eye, threw a shield over thee, by doing for thee one of these things taking pity on thee, - But thou wast cast out on the face of the field Because thy person, was abhorred, in the day thou wast born.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
And I passed by thee, and looked upon thee, thrusting about thee in thy blood, And said to thee— Despite thy blood, live! Yea I said to thee— Despite thy blood, live!
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Into myriads—like the bud of the field, made I thee, And thou didst increase and become well grown, and didst attain to most excellent adornments, — Thy breasts were well-formed And thy hair was grown, But thou thyself wast utterly naked.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
And I passed by thee and looked upon thee and lo! thy time was the time for endearments, So I spread my skirt over thee, and covered thy shame, And took an oath to thee And entered into covenant with thee. Declareth My Lord. Yahweh. And thou didst become mine.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
And I bathed thee in water, and rinsed thy blood from off thee, And anointed thee with oil;
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
And clothed thee with an embroidered dress, And sandalled thee in red leather, And wrapped thee about with fine linen, And put over thee a mantle of silk.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
Then decked I thee with ornaments, And put bracelets upon thy hands, And a neckchain upon thy throat;
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
And put a nose-jewel upon thy nose, And earrings in thine ears, And a crown of adorning, upon thy head.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Thus wast thou adorned with gold and silver, And thy raiment was of fine linen and silk and embroidered work, Fine flour and honey and oil, didst thou eat, — And so thou becamest exceedingly beautiful, And didst attain unto royalty.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
Then went forth thy fame among the nations. for thy beauty, - For perfect, it was—in my splendour which I had put upon thee, Declareth My Lord, Yahweh.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
Then didst thou trust in thy beauty, And become unchaste, because of thy fame, - And didst pour out thine unchastity upon every passer-by, his it was!
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
Yea thou didst take of thy raiment and madest thee high places of hangings, And didst commit unchastity thereon, - Which ought not to have befallen And not to have come to pass.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
But thou didst take thine adorning jewels Of my gold and of my silver which I had given thee, And didst make thee images of the male, — And didst act unchastely with them;
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
And thou didst take thine embroidered raiment, and cover them, - And mine oil and mine incense, didst thou set before them;
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And my food which I had given thee, Fine flour and oil and honey wherewith I fed thee, And didst set it before them for a satisfying odour Yea so it was, — Saith My Lord Yahweh.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
And thou didst take thy sons and thy daughters, Whom thou hadst borne unto me, And didst sacrifice them unto them to be devoured, - Is this of thine unchastity. a light thing?
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
Yea thou didst slay my children, — And didst deliver them up. that they should be caused to pass through the fire unto them.
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
And in all thine abominations, and thine unchaste ways, thou rememberedst not the days of thy youth, When thou wast utterly naked. When thou wast thrusting about thee in thy blood!
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
And it came to pass after all thy wickedness, Woe! Woe! to thee, Exclaimeth My Lord Yahweh;
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
That thou didst build thee a brothel, — and didst make thee a height in every broadway:
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
At the head of every road, didst thou build thy height, And bring thy beauty into disgust, And open thy feet to every passer-by, So didst thou make thine unchaste ways to abound.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Then didst thou extend thine unchaste acts unto the sons of Egypt—thy neighbour great of flesh, - And caused thine unchaste ways to abound provoking me to anger.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Lo! therefore, I have stretched out my hand against thee, And diminished thine allotted portion, — And have delivered thee up unto the desire of them who hate thee The daughters of the Philistines, who are ashamed of thy lewd way.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Thou didst also extend thine unchastity unto the sons of Assyria, because thou wast insatiable. Yet though thou didst behave unchastely with them, yet even so couldst thou not be satisfied,
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Thou didst therefore cause thine unchaste ways to abound unto the land of Canaan as towards Chaldea. Yet even herewith, wast thou not satisfied.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
How weak was thy heart! Exclaimeth My Lord Yahweh, — That thou couldst have done all these things, The doing of a lewd woman without shame:
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
That thou couldst have built thy brothel at the head of every road, And thy height, couldst have made in every broadway, - Yet becamest not as a harlot to lay claim to a harlot’s hire.
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
A wife who committeth adultery, instead of her husband accepteth strangers.
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
To all harlots, they give a present, — But, thou, didst give thy presents to all thy lovers, And didst bribe them to come in unto thee from every side, in thine unchastity!
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
And so there came about in thee, the reverse of women, in thine unchastity, In that they did not follow thee for purposes of lewdness, — And in that thou gavest a present while, no present, was given to thee So didst thou become, the reverse.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
Therefore O harlot, hear thou the word of Yahweh;
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Thus saith My Lord Yahweh, — Because thy money, was poured out, and thy shame, was uncovered, in thine unchastity, unto thy lovers, —and unto all thine abominable manufactured gods, even as the blood of thy children, whom thou didst deliver up unto them,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
Therefore behold me! gathering together all thy lovers unto whom thou didst make thyself pleasant, Even all whom thou lovedst, With all whom thou hatedst, — Yea I will gather them together unto thee from every side And will uncover thy shame unto them, And they shall see all thy shame.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
So will I judge thee. with the judgments meted out to adulteresses and shedders of blood, - And will repay thee with the blood of indignation and jealousy;
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
And will deliver thee into their hand. And they shall pull down thy brothel And break in pieces thy heights, And strip thee of thy raiment, And take away thine adorning jewels, - And leave thee utterly naked.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
Then will they bring up against thee a gathered host, And they will stone thee with stones, - And cut thee to pieces with their swords;
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
And burn up thy houses with fire, And execute upon thee judgments before the eyes of many women, —So will I cause thee to cease from acting unchastely, Moreover also a present, shalt thou not give any more.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
So will I let mine indignation find rest in thee, And my jealousy shall depart from thee, —And I will be quiet, and not be provoked any more.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
Because thou hast not remembered the days of thy youth, But hast enraged me with all these things Therefore also behold! I thy way, upon thine own head, will place Declareth My Lord Yahweh, And thou shalt not commit a crime above all thine abominations
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Lo! every one who useth proverbs, against thee, shall use a proverb saying, — Like the mother, so her daughter!
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
The daughter of thy mother, thou art! One abhorring her own husband and her own children, — Yea the sister of thy sisters, thou art Who abhorred their own husbands and their own children, Your mother was a Hittite, And your father an Amorite.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
And thine elder sister, was Samaria, she and her daughters, dwelling on thy left hand, — And thy sister younger than thou dwelling on thy right hand was Sodom and her daughters.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Yet not in their ways, didst thou walk, nor according to their abominations, didst thou do, — As though that were quite too little, thou didst corrupt thyself beyond them in all thy ways.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
As I live, Declareth My Lord Yahweh, Very! Sodom thy sister had not done, neither she nor her daughters, —as thou and thy daughters have done.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Lo! this became the iniquity of Sodom thy sister, — Pride, fulness of bread, and careless security came to her and to her daughters, And the hand of the oppressed and the needy, she strengthened not.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
So then they became haughty, and committed abomination before me, - And I took them away. when I saw [it],
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Nor did, Samaria, commit, one-half thy sins, — But thou didst multiply thine abominations more than they, And didst cause thy sisters to appear righteous, by all the abominations which thou didst commit.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Thou also bear thine own reproach, which thou didst adjudge to thy sisters, by thy sins in which thou wast more abominable than they, thou didst make them appear more righteous than thou, — Thou also, therefore turn thou pale and bear thine own reproach, for making thy sisters appear righteous!
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
When therefore I bring back their captivity, The captivity of Sodom and her daughters, And the captivity of Samaria and her daughters Then will I bring back thy captivities in their midst:
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
That thou mayest bear thine own reproach, And take to thyself reproach because of all that thou didst in comforting them.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
When thy sisters Sodom and her daughters shall return to their former estate, And Samaria and her daughters shall return to their former estate Then thou and thy daughters, shall return to your former estate.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
And Sodom thy sister was never heard in thy mouth, —In the day of thy pride:
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
Before thy wickedness was discovered, As now, [thou art] the reproach of the daughters of Syria and all round about her the daughters of the Philistines, —who are despising thee on every side.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
As for thy crime and thine abominations, thou thyself, dost bear them, — Declareth Yahweh.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
For Thus, saith My Lord, Yahweh, Therefore will I deal with thee just as thou hast dealt, - In that thou didst despise an oath by breaking a covenant.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Therefore will I remember my covenant with thee in the days of thy youth, — And will establish for thee a covenant age-abiding.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Thou shalt therefore remember thy ways and take to thyself reproach, by receiving thy sisters. The older than thou, And the younger than thou, - And I will give them unto thee for daughters Though not by thine own covenant.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
But I myself, will establish my covenant with thee— And thou shalt know that I, am Yahweh:
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
To the end thou mayest remember and turn pale, and there be to thee no more, an opening of mouth, because of thy reproach, - In that I have accepted a propitiatory covering for thee as to all that thou hast done, Declareth My Lord. Yahweh.