< Ezekieli 15 >
1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
Dis, fils de l'homme, qu'est-ce que le bois de la vigne, en comparaison des arbres qui se trouvent dans les forêts?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Prendra-t-on le bois pour le rendre propre à être mis en œuvre? En fera- t-on des chevilles pour y suspendre quelque objet?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Il n'est bon qu'à être jeté au feu et consumé; le feu chaque année consume le sarment qu'on ôte à la vigne en la taillant, et finalement il n'en reste rien; est-ce qu'il est propre à être mis en œuvre?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Et même lorsqu'il est encore entier, il ne peut servir à aucune œuvre: si donc le feu l'a entièrement consumé, sera-t-il propre à être mis en œuvre?
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
À cause de cela, dis-leur: Ainsi parle le Seigneur: De même que j'ai abandonné au feu, pour être consumé, le bois de la vigne parmi les arbres de la forêt; ainsi j'ai abandonné les habitants de Jérusalem.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Et je tournerai contre eux mon visage; ils sortiront du feu, et cependant le feu les dévorera, et ils sauront que je suis le Seigneur, lorsque j'aurai tourné mon visage contre eux.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
Et je livrerai leur terre à la désolation pour les punir de leurs transgressions, dit le Seigneur.