< Ezekieli 14 >

1 Tsiku lina ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kwa ine ndipo anakhala pansi pamaso panga.
Et quelques-uns des anciens du peuple d'Israël vinrent me trouver, et ils s'assirent devant moi.
2 Ndipo Yehova anandipatsa uthenga uwu nati,
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
3 “Iwe mwana wa munthu, anthu awa ayika mtima pa mafano awo. Ayikanso maso awo pa zinthu zina zoyipa zopunthwitsa. Kodi ayembekezera kuti ndiwayankhe chimene atandifunse?
Fils de l'homme, ces hommes ont conçu leurs pensées en leurs cœurs, et ils ont mis devant leur visage la punition de leurs iniquités: que dois-je leur répondre?
4 Tsono yankhula nawo ndi kuwawuza kuti zimene akunena Ambuye Yehova: ‘Ngati Mwisraeli aliyense ayika mtima wake pa mafano ndi kuyika maso ake pa zinthu zoyipa zopunthwitsa, kenaka nʼkupita kwa mneneri, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha molingana ndi kuchuluka kwa mafano ake.
Parle et dis-leur: Voici ce que dit le Seigneur: Tout homme, un homme d'Israël, qui aura conçu des pensées en son cœur et qui aura mis devant son visage la punition de son iniquité, et qui viendra devant le prophète, moi le Seigneur je lui répondrai selon les engagements de sa pensée.
5 Ine ndidzachita zimenezi kuti mwina nʼkukopa mitima ya anthu a Israeli, amene andisiya chifukwa cha mafano awo.’
Car il désire tromper la maison d'Israël, pour qu'elle se laisse entraîner par ses convoitises et qu'elle éloigne son cœur de moi.
6 “Nʼchifukwa chake uwawuze Aisraeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Lapani! Siyani mafano anu ndi ntchito zanu zonse zonyansa!
À cause de cela, dis à la maison d'Israël: Ainsi parle le Seigneur: Convertissez-vous et détournez-vous de vos mauvaises œuvres et de toutes vos iniquités, et détournez-en vos visages.
7 “‘Ngati Mwisraeli wina aliyense kapena mlendo wina aliyense wokhala pakati pa Israeli adzichotsa yekha kwa Ine ndi kuyika mtima pa mafano ake ndi kuyikanso maso ake pa zinthu zopunthwitsa ndipo kenaka nʼkupita kwa mneneri kukafunsa nzeru, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha.
Car tout homme, un homme de la maison d'Israël, et tout étranger prosélyte en Israël, qui se sera éloigné de moi et aura conçu des pensées en son cœur et aura mis devant son visage la punition de son iniquité, et qui viendra ensuite au prophète pour le questionner sur moi, moi le Seigneur, je lui répondrai selon les engagements où il est lui-même.
8 Ine ndidzalimbana naye munthu ameneyo ndipo ndidzamusandutsa chitsanzo ndi chisudzo. Ndidzamuchotsa pakati pa anthu anga. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Et je tournerai mon visage contre cet homme, et je le livrerai à la solitude et à l'extermination, et je l'effacerai du milieu de mon peuple, et vous saurez que je suis le Seigneur.
9 “‘Ndipo ngati mneneri anyengedwa nanenera, Ine Yehova ndiye ndamunyenga mneneri ameneyo, ndipo ndidzatambasula dzanja langa kumukantha ndi kumuwononga pakati pa anthu anga Aisraeli.
Et si un prophète s'est égaré, et s'il a parlé, c'est moi le Seigneur qui ai égaré ce prophète; et j'étendrai la main sur lui, et je l'exterminerai du milieu de mon peuple d'Israël.
10 Iwo adzalangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Chilango cha wodzafunsira nzeru kwa mneneri chidzafanana ndi chilango cha mneneriyo.
Et ils porteront la peine de leur iniquité, selon l'iniquité de celui qui aura interrogé, laquelle sera punie de la même manière que l'iniquité du prophète;
11 Ndidzachita zimenezi kuti Aisraeli asasocherenso kundisiya Ine ndi kuti asadziyipitsenso ndi machimo awo. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, akutero Ambuye Yehova.’”
Afin que la maison d'Israël ne s'égare plus en s'éloignant de moi, qu'elle ne se souille plus par ses péchés; de sorte qu'elle soit mon peuple, et que je sois son Dieu, dit le Seigneur.
12 Yehova anayankhula nane kuti,
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
13 “Iwe mwana wa munthu, ngati dziko lindichimwira posandikhulupirira, Ine ndidzatambasula dzanja langa kulikantha pochepetsa chakudya chake. Ndidzatumiza njala pa dzikolo ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Fils de l'homme, la terre qui aura péché contre moi en ses transgressions, j'étendrai la main sur elle; je briserai la force du pain, je lui enverrai la famine, et je détruirai les hommes et son bétail.
14 Ngakhale anthu atatu awa, Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, akanangopulumutsa moyo wawo chifukwa cha chilungamo chawo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et si, au milieu d'elle, se trouvent trois hommes comme Noé, Daniel et Job, ils seront sauvés à cause de leur justice, dit le Seigneur.
15 “Kapena ndikanatumiza zirombo mʼdziko monse ndi kulisiya lopanda anthu, ndipo dzikolo nʼkukhala chipululu chakuti munthu sangadutse chifukwa cha zirombo.
Et si j'amène les bêtes farouches sur cette terre, et si je la punis, et si elle est désolée, et que nul ne la traverse en face des bêtes farouches;
16 Apanso, ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo okha akanapulumuka, koma dziko likanasanduka chipululu.’
Si ces trois hommes s'y trouvent, par ma vie, dit le Seigneur, ni leurs fils ni leurs filles ne seront sauvés; eux seuls seront sauvés, mais la terre sera détruite.
17 “Kapena ndikanatumiza lupanga mʼdzikolo ndi kunena kuti, ‘Lupanga lipite mʼdziko monse,’ ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Ou bien encore, si je promène le glaive sur cette terre, et si je dis: Que le glaive sillonne toute cette terre, et j'en ôterai les hommes et le bétail;
18 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna kapena ana aakazi. Iwo okha akanapulumuka.’
Et si ces trois hommes s'y trouvent, par ma vie, dit le Seigneur, ils ne sauveront ni leurs fils ni leurs filles; eux seuls seront sauvés.
19 “Kapena ndikanatumiza mliri mʼdzikomo ndi kuonetsa ukali wanga pokhetsa magazi, kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Ou bien encore, si j'envoie la peste en cette terre, et si je verse sur elle ma colère, avec le sang, pour détruire ses hommes et son bétail,
20 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti ngakhale Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, sakanatha ngakhale kupulumutsa mwana wamwamuna kapena wamkazi. Akanangodzipulumutsa okha chifukwa cha chilungamo chawo.
Et si Noé, Daniel et Jacob s'y trouvent, par ma vie, dit le Seigneur, ni leurs fils ni leurs filles n'échapperont; eux seuls, à cause de leur justice, auront sauvé leurs âmes.
21 “Pakuti Ambuye Yehova akuti: Kudzakhala zoopsa kwambiri pamene ndidzatumiza pa Yerusalemu zilango zanga zinayi izi: lupanga, njala, zirombo ndi mliri kuti ziwononge anthu ake ndi nyama zomwe!
Voici ce que dit le Seigneur: Si j'envoie contre Jérusalem les quatre fléaux: le glaive, la famine, les bêtes farouches et la peste, pour y détruire les hommes et le bétail;
22 Komabe padzakhala ena opulumuka, ana aamuna ndi ana aakazi amene adzatulutsidwa mʼdzikomo. Iwo adzabwera kwa inu, ndipo mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo, mitima yanu idzakhala pansi mukadzakumbukira chilango chimene ndinachita pa Yerusalemu.
Voilà qu'il restera quelques hommes; et ceux-là seront sauvés; et ils emmèneront de la ville leurs fils et leurs filles; puis voilà qu'ils viendront à vous, et vous verrez leurs voies et leurs pensées; et le repentir vous pénètrera, à cause des maux que j'aurai fait tomber sur Jérusalem, à cause de toutes les afflictions que je lui aurai envoyées.
23 Mitima yanu idzakhala pansi mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo. Tsono mudzadziwa kuti Yerusalemu sindinamuchite zimenezi popanda chifukwa, akutero Ambuye Yehova.”
Et ils vous consoleront, parce que vous verrez leurs voies et leurs pensées; et vous reconnaîtrez que ce n'est point à tort que j'ai fait tout ce que j'ai fait contre elle, dit le Seigneur.

< Ezekieli 14 >