< Eksodo 9 >
1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
And he said Yahweh to Moses go to Pharaoh and you will say to him thus he says Yahweh [the] God of the Hebrews let go people my so they may serve me.
2 Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
That except [are] refusing you to let [them] go and still you [are] keeping hold on them.
3 dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
There! [the] hand of Yahweh [is] about to be on livestock your which [is] in the field on the horses on the donkeys on the camels on the cattle and on the sheep a pestilence heavy very.
4 Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
And he will separate Yahweh between [the] livestock of Israel and between [the] livestock of Egypt and not it will die of all [that belongs] to [the] people of Israel anything.
5 Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
And he set Yahweh an appointed time saying tomorrow he will do Yahweh the thing this in the land.
6 Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
And he did Yahweh the thing this from [the] next day and it died all [the] livestock of Egypt and of [the] livestock of [the] people of Israel not it died one.
7 Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
And he sent Pharaoh and there! not it had died any of [the] livestock of Israel up to one and it was unresponsive [the] heart of Pharaoh and not he let go the people.
8 Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
And he said Yahweh to Moses and to Aaron take for yourselves [the] fullness of hands your soot of a furnace and he will sprinkle it Moses the heavens towards to [the] eyes of Pharaoh.
9 Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
And it will become dust over all [the] land of Egypt and it will become on humankind and on the livestock boil[s] breaking out blisters in all [the] land of Egypt.
10 Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
And they took [the] soot of the furnace and they stood before Pharaoh and he sprinkled it Moses the heavens towards and it became boil[s] blisters breaking out on humankind and on the livestock.
11 Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
And not they were able the magicians to stand before Moses because of the boil[s] for it was the boil[s] on the magicians and on all Egypt.
12 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
And he made strong Yahweh [the] heart of Pharaoh and not he listened to them just as he had said Yahweh to Moses.
13 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
And he said Yahweh to Moses rise early in the morning and present yourself before Pharaoh and you will say to him thus he says Yahweh [the] God of the Hebrews let go people my so they may serve me.
14 Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
For - at the time this I [am] about to send all plagues my to heart your and on servants your and on people your in order that you may know that there not [is] like me in all the earth.
15 Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
For now I stretched out hand my and I struck you and people your with pestilence and you were destroyed from the earth.
16 Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
And but for sake of this I have caused to stand you in order to see you power my and so as to recount name my in all the earth.
17 Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
Still you [are] exalting yourself on people my to not to let go them.
18 Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
Here I [am] about to rain down about this time tomorrow hail heavy very which not it has been like it in Egypt from the day was founded it and until now.
19 Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
And therefore send bring to refuge livestock your and all that [belongs] to you in the field all the humankind and the livestock which it will be found in the field and not it will be gathered the house towards and it will come down on them the hail and they will die.
20 Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
The [one] fearing [the] word of Yahweh of [the] servants of Pharaoh he made to flee servants his and livestock his into the houses.
21 Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
And [the one] who not he set heart his to [the] word of Yahweh and he left servants his and livestock his in the field.
22 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
And he said Yahweh to Moses stretch out hand your to the heavens so may it be hail in all [the] land of Egypt on the humankind and on the livestock and on all [the] vegetation of the field in [the] land of Egypt.
23 Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
And he stretched out Moses staff his to the heavens and Yahweh he gave thunder claps and hail and it went fire [the] ground towards and he rained down Yahweh hail on [the] land of Egypt.
24 Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
And it was hail and fire [was] flashing in [the] middle of the hail heavy very which not it had been like it in all [the] land of Egypt from then it had become a nation.
25 Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
And it struck the hail in all [the] land of Egypt all that [was] in the field from humankind and unto livestock and all [the] vegetation of the field it struck the hail and every tree of the field it shattered.
26 Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
Only in [the] land of Goshen where [were] there [the] people of Israel not it was hail.
27 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
And he sent Pharaoh and he summoned Moses and Aaron and he said to them I have sinned this time Yahweh [is] the righteous [one] and I and people my [are] the guilty [ones].
28 Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
Pray to Yahweh and [is too] much for being [the] thunder claps of God and [the] hail and I will let go you and not you will increase! to stay.
29 Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
And he said to him Moses when have gone out I the city I will spread out hands my to Yahweh the thunder claps they will cease! and the hail not it will happen again so that you may know that [belongs] to Yahweh the earth.
30 Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
And you and servants your I know that not yet you fear! because of Yahweh God.
31 Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
And the flax and the barley it was struck for the barley [was] young barley ear[s] and the flax [was] bud.
32 Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
And the wheat and the spelt not they were struck for [are] late [crops] they.
33 Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
And he went out Moses from with Pharaoh the city and he spread out hands his to Yahweh and they ceased the thunder claps and the hail and rain not it was poured out [the] earth towards.
34 Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
And he saw Pharaoh that it had ceased the rain and the hail and the thunder claps and he repeated to sin and he made heavy heart his he and servants his.
35 Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
And it was strong [the] heart of Pharaoh and not he let go [the] people of Israel just as he had said Yahweh by [the] hand of Moses.