+ Genesis 1 >
1 Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
In beginning he created God the heavens and the earth.
2 Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
And the earth was formlessness and emptiness and darkness [was] over [the] surface of [the] deep and [the] spirit of God [was] hovering over [the] surface of the waters.
3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
And he said God let it be light and there was light.
4 Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
And he saw God the light that [it was] good and he separated God between the light and between the darkness.
5 Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
And he called God - the light day and the darkness he called night and there was evening and there was morning day one.
6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
And he said God let it be a firmament in [the] middle of the waters and let it be separating between waters to waters.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
And he made God the firmament and he separated between the waters which [were] from under to the firmament and between the waters which [were] from the firmament and it was so.
8 Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
And he called God the firmament heaven and there was evening and there was morning a day second.
9 Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
And he said God let them gather the waters from under the heavens to a place one and let it appear the dry ground and it was so.
10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And he called God - the dry ground earth and [the] collection of the waters he called seas and he saw God that [it was] good.
11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
And he said God let it sprout the earth vegetation plant[s] [which] bears seed seed tree[s] of fruit producing fruit to kind its which seed its [is] in it on the earth and it was so.
12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And brought forth the earth vegetation plant[s] [which] bears seed seed to kind its and tree[s] (producing *LAH(b)*) fruit which seed its [was] in it to kind its and he saw God that [it was] good.
13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
And there was evening and there was morning a day third.
14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
And he said God let it be luminaries in [the] firmament of the heavens to separate between the day and between the night and they will become signs and appointed times and days and years.
15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
And they will become luminaries in [the] firmament of the heavens to give light on the earth and it was so.
16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
And he made God [the] two the luminaries great the luminary great for [the] dominion of the day and the luminary small for [the] dominion of the night and the stars.
17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
And he set them God in [the] firmament of the heavens to give light on the earth.
18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And to rule over the day and over the night and to separate between the light and between the darkness and he saw God that [it was] good.
19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
And there was evening and there was morning a day fourth.
20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
And he said God let them swarm the waters swarming thing[s] creature[s] living and bird[s] let it fly above the earth on [the] surface of [the] firmament of the heavens.
21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And he created God the sea monsters great and every creature living - which creeps which they swarmed the waters to kind their and every bird of wing to kind its and he saw God that [it was] good.
22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
And he blessed them God saying be fruitful and multiply and fill the waters in the seas and the bird[s] let it multiply on the earth.
23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
And there was evening and there was morning a day fifth.
24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
And he said God let it produce the earth creature[s] living to kind its livestock and creeping thing[s] and animal[s] of [the] earth to kind its and it was so.
25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
And he made God [the] animal[s] of the earth to kind its and the livestock to kind its and every creeping thing of the ground to kind its and he saw God that [it was] good.
26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
And he said God let us make humankind in image our according to likeness our and they may rule over [the] fish of the sea and over [the] bird[s] of the heavens and over the livestock and over all the earth and over every creeping thing which creeps on the earth.
27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
And he created God - humankind in own image his in [the] image of God he created it male and female he created them.
28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
And he blessed them God and he said to them God be fruitful and multiply and fill the earth and subdue it and rule over [the] fish of the sea and over [the] bird[s] of the heavens and over every animal which creeps on the earth.
29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
And he said God here! I give to you every plant - [which] bears seed seed which [is] on [the] surface of all the earth and every tree which in it [is the] fruit of a tree [which] bears seed seed to you will be[long] to food.
30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
And to every animal of the earth and to every bird of the heavens and to every - creeping [thing] on the earth which [is] in it life living all greenery of plant[s] to food and it was so.
31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.
And he saw God all that he had made and there! [it was] good very and there was evening and there was morning [the] day sixth.