< Eksodo 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
And he said Yahweh to Moses now you will see [that] which I will do to Pharaoh for by a hand strong he will let go them and by a hand strong he will drive out them from land his.
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
And he spoke God to Moses and he said to him I [am] Yahweh.
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
And I appeared to Abraham to Isaac and to Jacob God Almighty and name my Yahweh not I made myself known to them.
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
And also I established covenant my with them to give to them [the] land of Canaan [the] land of sojournings their which they sojourned in it.
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
And also - I I have heard [the] groaning of [the] people of Israel whom Egypt [are] compelling to labor them and I have remembered covenant my.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Therefore say to [the] people of Israel I [am] Yahweh and I will bring out you from under [the] forced labor of Egypt and I will deliver you from labor their and I will redeem you by an arm outstretched and with acts of judgment great.
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
And I will take you for myself to a people and I will become for you God and you will know that I [am] Yahweh God your who brought out you from under [the] forced labor of Egypt.
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
And I will bring you into the land which I lifted up hand my to give it to Abraham to Isaac and to Jacob and I will give it to you a possession I [am] Yahweh.
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
And he spoke Moses thus to [the] people of Israel and not they listened to Moses from shortness of spirit and from labor hard.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
Go speak to Pharaoh [the] king of Egypt so he may let go [the] people of Israel from land his.
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
And he spoke Moses before Yahweh saying here! [the] people of Israel not they have listened to me and how? will he listen to me Pharaoh and I [am] uncircumcised of lips.
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
And he spoke Yahweh to Moses and to Aaron and he commanded them to [the] people of Israel and to Pharaoh [the] king of Egypt to bring out [the] people of Israel from [the] land of Egypt.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
These [were] [the] heads of [the] household of ancestors their [the] sons of Reuben [the] firstborn of Israel [were] Hanoch and Pallu Hezron and Carmi these [were] [the] clans of Reuben.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
And [the] sons of Simeon [were] Jemuel and Jamin and Ohad and Jakin and Zohar and Shaul [the] son of Canaanite [woman] these [were] [the] clans of Simeon.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And these [were] [the] names of [the] sons of Levi to descendants their Gershon and Kohath and Merari and [the] years of [the] life of Levi [were] seven and thirty and one hundred year[s].
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
[the] sons of Gershon [were] Libni and Shimei to clans their.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
And [the] sons of Kohath [were] Amram and Izhar and Hebron and Uzziel and [the] years of [the] life of Kohath [were] three and thirty and one hundred year[s].
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
And [the] sons of Merari [were] Mahli and Mushi these [were] [the] clans of the Levite[s] to descendants their.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And he took Amram Jochebed father's sister his for himself to a wife and she bore to him Aaron and Moses and [the] years of [the] life of Amram [were] seven and thirty and one hundred year[s].
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
And [the] sons of Izhar [were] Korah and Nepheg and Zikri.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
And [the] sons of Uzziel [were] Mishael and Elzaphan and Sithri.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
And he took Aaron Elisheba [the] daughter of Amminadab [the] sister of Nahshon for himself to a wife and she bore to him Nadab and Abihu Eleazar and Ithamar.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
And [the] sons of Korah [were] Assir and Elkanah and Abiasaph these [were] [the] clans of the Korahite[s].
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
And Eleazar [the] son of Aaron he took for himself one of [the] daughters of Putiel for himself to a wife and she bore to him Phinehas these [were] [the] heads of [the] ancestors of the Levites to clans their.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
That Aaron and Moses whom he said Yahweh to them bring out [the] people of Israel from [the] land of Egypt on hosts their.
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
They [were] the [ones who] were speaking to Pharaoh [the] king of Egypt to bring out [the] people of Israel from Egypt that Moses and Aaron.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
And it was on [the] day [when] he spoke Yahweh to Moses in [the] land of Egypt.
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
And he spoke Yahweh to Moses saying I [am] Yahweh speak to Pharaoh [the] king of Egypt all that I [am] speaking to you.
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
And he said Moses before Yahweh here! I [am] uncircumcised of lips and how? will he listen to me Pharaoh.

< Eksodo 6 >